Masalimo 45 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 45:1-17

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;

iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.

11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;

mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.

12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,

amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,

chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.

14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;

anamwali okhala naye akumutsatira

ndipo abweretsedwa kwa inu.

15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;

akulowa mʼnyumba yaufumu.

16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;

udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.

17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;

choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

Korean Living Bible

시편 45:1-17

왕의 결혼에 대한 노래

(고라 자손의 교훈시. 성가대 지휘자를 따라 ‘백합화’ 곡조에 맞춰 부른 사랑의 노래)

1내 마음이 아름다운

시상에 젖어

왕을 위해 이 가사를 지으니

내 혀가 훌륭한 작가의

붓과 같구나.

2왕은 사람들 중에서도

가장 아름답고

그 입술로 은혜를 베푸시니

하나님이 언제나

왕을 축복해 주셨습니다.

3힘 있는 자시여,

허리에 칼을 차고

영광과 위엄의 옷을 입으소서.

4왕은 진리와 겸손과 의를 위해

위엄 있게 말을 타고 승리하소서.

왕의 오른손으로

놀라운 일을 행하소서.

5왕의 화살이 날카로워

그 원수들의 심장을 꿰뚫으므로

만민이 왕의 발 앞에 엎드립니다.

6하나님이시여,

45:6 또는 ‘주의 보좌가 영영하며 주의 나라의 홀은 공평한 홀이니이다’주는 영원히 통치하시고

주의 나라를

정의의 지팡이로 다스리십니다.

7왕이 옳은 것을 사랑하고

악한 것을 미워하시므로

왕의 하나님은

왕에게 기쁨의 기름을 부어

다른 왕들보다 높이셨습니다.

8왕의 모든 옷은

몰약과 침향과

계피의 향기를 풍기고

상아궁에서 흘러나오는

현악기의 연주 소리는

왕의 마음을 즐겁게 합니다.

9왕이 거느린 여인들 가운데는

여러 나라의 공주들이 있으며

왕의 우편에는

오빌의 순금으로 단장한

왕후가 서 있습니다.

10딸이여, 내 말을 듣고

생각하며 귀를 기울여라.

너의 친정집 식구들을

다 잊어버려라.

11그러면 왕이 너의 아름다움을

기뻐할 것이다. 왕을 공경하라.

그는 너의 주가 되신다.

12두로 사람들이

너에게 선물을 가져오고

부유한 백성들도

너의 환심을 사려고 할 것이다.

13공주가 왕궁에서

모든 영화를 누리니

그 옷은 금으로 수놓았구나.

14수놓은 옷을 입은 공주가

왕에게 이끌려가며

시중드는 그녀의 친구 처녀들도

왕에게 이끌려가리라.

15저들이 기쁨과 즐거움으로

인도를 받아 왕궁으로 들어가리라.

16왕의 아들들이

왕의 조상들을 대신할 것이며

왕은 저들을 온 세계의 통치자로

삼으실 것입니다.

17내가 왕의 이름을 만대에

기억나게 할 것이므로

세상 민족들이

영원히 왕을 찬양할 것입니다.