Masalimo 45 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 45:1-17

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;

iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.

11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;

mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.

12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,

amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,

chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.

14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;

anamwali okhala naye akumutsatira

ndipo abweretsedwa kwa inu.

15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;

akulowa mʼnyumba yaufumu.

16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;

udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.

17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;

choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

Hoffnung für Alle

Psalm 45:1-18

Zur Hochzeit des Königs

1Von den Nachkommen Korachs, zum Nachdenken. Nach der Melodie: »Lilien«, ein Liebeslied.

2Mein Herz ist von Freude erfüllt,

ein schönes Lied will ich für den König singen.

Wie ein Dichter seine Feder,

so gebrauche ich meine Zunge für ein kunstvolles Lied:

3Du bist schön und stattlich wie kein anderer!

Freundlich und voller Güte sind deine Worte.

Jeder kann sehen, dass Gott dich für immer reich beschenkt hat.

4Gürte dein Schwert um, du tapferer Held!

Zeige deine königliche Majestät und Pracht!

5Sei stark und kämpfe für die Wahrheit;

regiere dein Volk umsichtig und gerecht!

Deine kühnen Taten sollen dir zum Sieg verhelfen.

6Deine spitzen Pfeile durchbohren das Herz deiner Feinde.

Ja, du wirst die Völker unterwerfen!

7Deine Herrschaft, o Gott, bleibt immer und ewig bestehen.45,7 Hier wird der König als Stellvertreter Gottes auf Erden angesprochen.

In deinem Reich herrscht vollkommene Gerechtigkeit,

8denn du liebst das Recht

und hasst das Böse.

Darum hat dich dein Gott als Herrscher eingesetzt,

er hat dich zum Zeichen dafür mit Öl gesalbt

und mehr als alle anderen mit Freude beschenkt.

9Alle deine Gewänder duften nach kostbarem Parfüm45,9 Wörtlich: nach Myrrhe, Aloe und Kassia..

Aus elfenbeinverzierten Palästen erklingen Harfen,

um dich mit ihrer Musik zu erfreuen.

10Selbst Königstöchter sind zu Gast an deinem Hof,45,10 Wörtlich: Königstöchter sind unter deinen Kostbarkeiten.

und an deiner rechten Seite steht die Gemahlin,

die sich mit dem feinsten Gold aus Ofir schmückt.

11Höre, Königstochter, und nimm dir meine Worte zu Herzen!

Vergiss dein Volk und deine Verwandten!

12Du bist wunderschön, und der König begehrt dich!

Verneige dich vor ihm, denn er ist dein Herr und Gebieter!

13Die Bewohner der Stadt Tyrus kommen mit Geschenken,

die Vornehmen und Reichen suchen deine Gunst.

14Seht, wie prachtvoll zieht die Königstochter in den Festsaal ein!

Ihr Kleid ist mit Fäden aus Gold durchwebt,

15in ihrem farbenfrohen Gewand wird sie zum König geführt;

und Brautjungfern, ihre Freundinnen, begleiten sie.

16Mit Freudenrufen und hellem Jubel

wird der feierliche Brautzug in den Palast geleitet.

17O König! Du wirst viele Söhne haben;

auch sie werden wie deine Vorfahren regieren.

Auf der ganzen Welt wirst du sie zu Herrschern einsetzen.

18Mein Lied wird deinen Ruhm durch alle Generationen tragen,

darum werden die Völker dich allezeit preisen.