Masalimo 45 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 45:1-17

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;

iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.

11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;

mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.

12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,

amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,

chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.

14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;

anamwali okhala naye akumutsatira

ndipo abweretsedwa kwa inu.

15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;

akulowa mʼnyumba yaufumu.

16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;

udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.

17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;

choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

Священное Писание

Забур 45:1-12

Песнь 45

1Дирижёру хора. Под аламот45:1 Аламот – неизвестный музыкальный термин, обозначающий, вероятнее всего, определённый стиль или верхний звуковой регистр.. Песнь потомков Кораха.

2Всевышний – прибежище нам и сила,

верный помощник в бедах.

3Потому и не устрашимся мы,

пусть даже дрогнет сама земля,

и горы обрушатся в бездну моря,

4пусть воды морские ревут и пенятся,

и горы дрожат от их волнения. Пауза

5Речные потоки радуют город Всевышнего45:5 То есть Иерусалим.,

святое жилище Высочайшего.

6Всевышний в этом городе, и он не падёт;

Всевышний поддерживает его с раннего утра.

7Народы мятутся, и царства рушатся;

подаёт Он Свой голос – и тает земля.

8С нами Вечный, Повелитель Сил;

Бог Якуба – наша крепость. Пауза

9Придите, посмотрите на дела Вечного,

какие опустошения Он произвёл на земле.

10До краёв земли прекращает Он войны,

ломает луки и копья

и сжигает дотла щиты45:10 Или: «колесницы»..

11Он говорит: «Остановитесь, познайте, что Я – Бог;

Я прославлюсь в народах,

прославлюсь на земле».

12С нами Вечный, Повелитель Сил;

Бог Якуба – наша крепость. Пауза