Masalimo 44 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

Nueva Versión Internacional

Salmo 44:1-26

Salmo 44Sal 44 En el texto hebreo 44:1-26 se numera 44:2-27.

Al director musical. Masquil de los hijos de Coré.

1Oh Dios, nuestros oídos han oído

y nuestros antepasados nos han contado

las proezas que realizaste en sus días,

en aquellos tiempos pasados:

2Con tu propia mano expulsaste a las naciones

y en su lugar plantaste a nuestros antepasados;

aplastaste a aquellos pueblos,

y a nuestros antepasados los hiciste prosperar.44:2 los hiciste prosperar. Lit. los libraste.

3Porque no fue su espada la que conquistó la tierra

ni fue su brazo el que les dio la victoria:

fue tu brazo, tu mano derecha;

fue la luz de tu rostro, porque tú los amabas.

4Solo tú eres mi Rey y mi Dios.

¡Decreta las victorias de Jacob!

5Por ti derrotamos a nuestros enemigos;

en tu nombre aplastamos a nuestros agresores.

6Yo no confío en mi arco

ni puede mi espada darme la victoria;

7tú nos das la victoria sobre nuestros enemigos,

y dejas en vergüenza a nuestros adversarios.

8¡Por siempre nos gloriaremos en Dios!

¡Por siempre alabaremos tu nombre! Selah

9Pero ahora nos has rechazado y humillado;

ya no sales con nuestros ejércitos.

10Nos hiciste retroceder ante el enemigo;

nos han saqueado nuestros adversarios.

11Nos has entregado para que nos devoren como ovejas

nos has dispersado entre las naciones.

12Has vendido a tu pueblo por una miseria

y nada has ganado con su venta.

13Nos has dejado en ridículo ante nuestros vecinos;

somos la burla y el escarnio de los que nos rodean.

14Nos has hecho el hazmerreír de las naciones;

todos los pueblos se burlan de nosotros.

15La humillación no me deja un solo instante;

se me cae la cara de vergüenza

16por las burlas de los que me insultan y me ofenden,

por culpa del enemigo que está presto a la venganza.

17Todo esto nos ha sucedido,

a pesar de que nunca te olvidamos

ni faltamos jamás a tu pacto.

18Nuestro corazón no ha vuelto atrás

ni nos hemos apartado de tu senda.

19Pero tú nos arrojaste a una cueva de chacales;

¡nos envolviste en la más tenebrosa oscuridad!

20Si hubiéramos olvidado el nombre de nuestro Dios

o extendido nuestras manos a un dios extraño,

21¿acaso Dios no lo habría descubierto,

ya que él conoce los más íntimos secretos?

22Por tu causa siempre nos llevan a la muerte;

¡nos tratan como a ovejas para el matadero!

23¡Despierta, Señor! ¿Por qué duermes?

¡Levántate! No nos rechaces para siempre.

24¿Por qué escondes tu rostro

y te olvidas de nuestro sufrimiento y opresión?

25Estamos abatidos hasta el polvo;

nuestro cuerpo se arrastra por el suelo.

26¡Levántate, ven a ayudarnos!

¡Por tu gran amor, rescátanos!