Masalimo 44 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

New Russian Translation

Псалтирь 44:1-18

Псалом 44

1Дирижеру хора. На мотив «Лилии». Наставление потомков Кораха. Свадебная песня44:1 Этот псалом использовался на коронацию царей Израиля. Иисус – окончательное исполнениее обещания о Царе Израиля – Мессии. Стихи 44:7-8 цитируются в Письме евреям Евр. 1:8-9 как относящиеся к Иисусу..

2Сердце мое прекрасной речью полнится.

Для Царя исполняю я эту песнь;

мой язык – перо искусного писаря.

3Ты прекраснее всех людей;

благодатная речь сходит с Твоих уст,

ведь Бог навеки благословил Тебя.

4Могучий, препояшься мечом,

облекись в славу и величие.

5И величия полон, победоносно поезжай верхом

ради истины, смирения и праведности.

Пусть рука Твоя вершит грозные подвиги.

6Пусть острые стрелы Твои пронзают сердца врагов царя;

пусть народы падут под ноги Твои.

7Вечен престол Твой, Боже,

Твой царский скипетр – скипетр правосудия.

8Ты возлюбил праведность, а беззаконие возненавидел;

поэтому, о Боже, Твой Бог помазал Тебя44:8 Или: «Поэтому Бог, Твой Бог, помазал Тебя».

маслом радости больше, чем Твоих сотоварищей44:7-8 Эти слова также являются пророчеством об Иисусе Христе (см. Евр. 1:8-9)..

9Благоухают Твои одежды миррой, алоэ и кассией44:9 Мирра (смирна) – приятно пахнущая смола растущего в Аравии растения. Алоэ – это источающее ароматную смолу дерево, родиной которого является Индокитай, использовалось как благовоние, а также при бальзамировании. Оно не имеет ничего общего с общеизвестным обыкновенным алоэ. Кассия – разновидность корицы..

Из дворцов, украшенных костью слоновой,

музыка струн Тебя веселит.

10Среди Твоих придворных женщин – царские дочери.

По правую руку от Тебя – царица в золоте из Офира.

11Выслушай, дочь, обдумай и прислушайся:

забудь свой народ и дом отца твоего.

12Царь возжелает твоей красоты,

покорись Ему – Он твой Господь.

13Жители Тира44:13 Букв.: «Дочь Тира». придут с дарами,

богатейшие из народа будут искать Твоей милости.

14Внутри этих покоев – дочь царя, невеста,

ее одежда золотом расшита44:14 Букв.: «Славна княжна внутри; шита золотом ее одежда»..

15В многоцветных одеждах выводят ее к Царю;

девушек, ее подруг, ведут к Царю вслед за ней.

16Их ведут с весельем и радостью;

они вступают в Царский дворец.

17Место предков Твоих, о44:17 В еврейском тексте этого слова нет. Царь, займут Твои сыновья;

по всей земле вождями Ты их поставишь.

18Я сделаю памятным имя Твое в поколениях,

и народы будут славить Тебя вовек.