Masalimo 44 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

Het Boek

Psalmen 44:1-27

1Een leerzaam gezang van de Korachieten voor de koordirigent.

2God, onze ouders hebben ons steeds weer verteld

hoe U in de geschiedenis met ons volk hebt gehandeld.

Wij hebben het zelf gehoord.

3Eigenhandig hebt U de volken weggejaagd

en onze voorouders in het land gezet.

U hebt andere volken verdrukt

en onze voorouders sterker laten worden.

4Zij hebben echt niet

zelf het land veroverd,

noch hun zwaard,

noch hun lichamelijke kracht

heeft hen bevrijd.

Uw kracht

en uw zorg

hebben dat gedaan,

omdat U hen liefhad.

5God, U bent mijn Koning,

zorgt U toch voor de verlossing van uw volk!

6In uw kracht vellen wij onze tegenstanders

en in uw naam lopen wij hen die tegen ons in opstand komen

onder de voet.

7Ik vertrouw niet op mijn boog

en verwacht geen verlossing van mijn zwaard.

8U hebt ons bevrijd van onze vijanden,

hen die ons haten hebt U voor schut gezet.

9Wij beroemen ons voortdurend op onze God,

uw naam zullen wij altijd prijzen.

10Toch hebt U ons weggestuurd en vernederd,

U bent niet meegegaan met onze legers toen die optrokken.

11U zorgde ervoor dat wij voor onze vijanden moesten wijken,

zij konden alles bij ons plunderen.

12U hebt ons overgeleverd als vee dat wordt geslacht.

Wij zijn onder andere volken verdeeld geraakt.

13U hebt uw volk voor een spotprijs van de hand gedaan,

van dat geld bent U niet rijk geworden.

14Onze buren roddelen over ons,

U hebt ons bespottelijk gemaakt voor hen die rondom ons wonen.

15Onze schande is spreekwoordelijk geworden bij andere volken,

ze schudden het hoofd om ons.

16Dag in, dag uit denk ik aan mijn schande,

ik durf mij niet meer te vertonen

17vanwege de woorden van de roddelaars

en de blikken van mijn vijanden en hen die op wraak uit zijn.

18Ondanks dit alles hebben wij U niet vergeten.

Ook hebben wij het verbond met U nooit ontkend.

19Ons hart bleef op U gericht,

wij bleven op het rechte pad.

20Desondanks hebt U ons op gevaarlijke plaatsen gebracht

en tastten wij soms geheel in het duister.

21Als wij uw naam hadden vergeten

en vreemde goden vereerd zouden hebben,

22zou God dat immers altijd merken?

Hij kent immers elke uithoek van het menselijk hart?

23Werkelijk, ter wille van U zijn wij voortdurend in levensgevaar,

wij worden beschouwd als schapen op weg naar het slachthuis.

24Word wakker! Waarom slaapt U, Here? Word toch wakker!

Laat ons toch niet meer in de steek.

25Waarom keert U ons de rug toe?

Waarom trekt U Zich onze ellende en moeiten niet aan?

26Wij stellen zelf niets meer voor

en liggen hulpeloos op de grond.

27Sta op, Here, en help ons, bevrijd ons ter wille van uw goedheid en liefde.