Masalimo 44 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

Священное Писание

Забур 44:1-18

Песнь 44

1Дирижёру хора. На мотив «Лилии». Наставление потомков Кораха. Свадебная песня.

2Сердце моё полнится прекрасной речью.

Для царя исполняю я эту песнь;

мой язык – перо искусного писаря.

3Ты прекраснее всех людей;

благодатная речь сходит с твоих уст,

ведь Всевышний навеки благословил тебя.

4Могучий, препояшься мечом,

облекись в славу и величие.

5И величия полон, победоносно поезжай верхом

ради истины, смирения и праведности.

Пусть рука твоя вершит грозные подвиги.

6Пусть острые стрелы твои пронзают сердца врагов царя;

пусть народы падут под ноги твои.

7О Боже, Твой престол вечен44:7 Или: «Вечен твой престол, что дан тебе Всевышним». В этом случае здесь на первый план выходит обращение к исраильскому царю, прообразу Масиха, и, значит, последующие местоимения будут писаться со строчной буквы.,

и справедливость – скипетр Твоего Царства.

8Ты возлюбил праведность, а беззаконие возненавидел;

поэтому Всевышний, Твой Бог, возвысил Тебя над другими,

помазав44:8 Посредством обряда помазания человек посвящался на определённое служение. Такого помазания удостаивались пророки, цари и священнослужители. Тебя при великой радости44:7-8 Эти слова являются пророчеством об Исе Масихе (см. Евр. 1:8-9)..

9Благоухают твои одежды миррой, алоэ и кассией44:9 Мирра (смирна) – приятно пахнущая смола растущего в Аравии растения. Алоэ – источающее ароматную смолу дерево, родиной которого является Индокитай, использовалось как благовоние, а также при бальзамировании. Не имеет ничего общего с общеизвестным обыкновенным алоэ. Кассия – разновидность корицы..

Из дворцов, украшенных костью слоновой,

музыка струн тебя веселит.

10Среди твоих почётных гостей – царские дочери.

По правую руку от тебя – царица в золоте из Офира.

11Выслушай, дочь, обдумай и прислушайся:

забудь свой народ и дом отца твоего.

12Царь возжелает твоей красоты,

покорись ему – он твой господин.

13Жители Тира придут с дарами,

богатейшие из народа будут искать твоей милости.

14Внутри покоев прекрасна невеста, дочь царя;

её одежда золотом расшита.

15В многоцветной одежде выводят её к царю;

девушки, её подруги, ведутся к тебе вслед за ней.

16Их ведут с весельем и радостью;

они вступают в царский дворец.

17Место предков твоих, о царь, займут твои сыновья;

по всей земле вождями ты их поставишь.

18Я сделаю памятным имя твоё в поколениях,

и народы будут славить тебя вовек.