Masalimo 44 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 44:1-27

Bøn efter et nederlag i krigen

1Til korlederen: En visdomssang af Koras slægt.

2Gud, vi har hørt om de mange undere,

du gjorde for vore forfædre i gamle dage.

3Du drev Kana’ans folk bort

og lod dit folk bosætte sig i deres land.

4De indtog ikke landet i egen kraft,

men du var med dem og hjalp dem.

5Du er vor Konge og Gud.

Giv fortsat sejr til dit folk.

6Med din hjælp får vi fjenderne under fod,

i dit navn besejrer vi vore modstandere.

7Vi stoler ikke på bue og sværd,

8for det er dig, der giver os sejr over fjenderne.

9Vi er stolte af at tilhøre dig, Gud,

vi vil prise dit navn for evigt.

10Hvordan kan det så være, at vi tabte slaget?

Hvorfor var du ikke med os i krigen?

Hvorfor har du forkastet os?

11Du tillod fjenden at drive os på flugt.

De plyndrede hele vores hær.

12Du udleverede os som får, der skal slagtes.

Du spredte os rundt blandt fremmede folk.

13Du solgte os for en slik,

regnede os ikke for noget.

14Vi blev til grin for nabofolkene,

de spotter og håner os.

15Selv fjerne folkeslag ler ad os

og ser på os med foragt.

16Vi føler os totalt ydmyget,

overvældet af skam.

17Vore fjender ser ned på os

og udslynger hån og spot.

18Hvordan kunne det ske, Gud?

Vi har da ikke svigtet dig

eller overtrådt den pagt, du oprettede med os.

19Vi har ikke været utro imod dig,

men har adlydt de bud, du gav os.

20Og dog blev vores by lagt i ruiner,

du sendte mørke og død over os.

21Hvis vi var holdt op med at tilbede dig, Gud,

og havde dyrket afguder i stedet,

22ville du da ikke vide besked?

Du kender jo vore inderste tanker.

23Men på trods af, at vi tilhører dig,

er vi i livsfare hver eneste dag.

Vi er som får, der er på vej til slagtning.

24Vågn op, Herre, hvorfor sover du?

Rejs dig, forkast os ikke længere!

25Hvorfor ser du den anden vej

og ignorerer vores nød og sorg?

26Vi ligger med ansigtet i støvet,

vore kroppe klæber til jorden.

27Grib ind, Herre, kom os til hjælp!

Red os i din trofasthed og nåde.