Masalimo 44 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

La Bible du Semeur

Psaumes 44:1-27

Rejetés par l’Eternel

1Au chef de chœur. Méditation44.1 Signification incertaine. des Qoréites44.1 Voir note 42.1..

2O Dieu, nous l’avons entendu ╵de nos propres oreilles,

nos pères nous ont raconté

tout ce que tu as accompli

de leur temps, autrefois.

3Par ton intervention, ╵tu as dépossédé des peuples ╵pour établir nos pères ;

et tu as frappé des peuplades ╵pour donner à nos pères ╵assez de place.

4Ce n’est pas grâce à leur épée ╵qu’ils ont occupé cette terre,

ni par leur propre force ╵qu’ils ont remporté la victoire :

mais c’est par ton action puissante,

car tu leur étais favorable ╵et les avais en affection.

5C’est toi, ô Dieu, qui es mon roi

et qui décides ╵le salut de Jacob44.5 Autre traduction : et qui fais triompher Jacob. Les anciennes versions grecque et syriaque ont lu : tu es mon roi, ô Dieu : ordonne le salut pour Jacob..

6Oui, avec toi ╵nous repoussons nos ennemis,

et grâce à toi ╵nous piétinons nos adversaires44.6 Voir 18.39 ; Jos 10.24 ; Es 51.23..

7Je ne compte pas sur mon arc,

mon épée ne me sauve pas,

8c’est toi, ô Dieu, ╵qui nous délivres ╵de tous nos ennemis

et qui couvres de honte ╵les gens qui nous haïssent.

9Tout au long de ce jour, ╵nous nous félicitons de Dieu ;

nous le louerons ╵jusqu’en l’éternité.

Pause

10Pourtant tu nous as rejetés

et livrés à la honte.

Tu as cessé d’accompagner ╵nos armées au combat !

11Tu nous fais reculer ╵devant nos ennemis :

nos adversaires ╵se sont emparés de nos biens.

12Oui, tu nous as livrés à eux, ╵ainsi qu’un troupeau de brebis ╵destinées à la boucherie,

et tu nous as éparpillés ╵parmi les peuples étrangers.

13Tu as vendu ton peuple ╵à un bas prix

sans en tirer aucun profit,

14et tu nous as livrés ╵aux railleries de nos voisins.

Tous ceux qui nous entourent ╵se rient et se moquent de nous.

15Tu fais de nous ╵la risée d’autres peuples.

En nous voyant, les étrangers ╵secouent la tête en ricanant.

16Tout le jour je vois mon humiliation,

et mon visage ╵est marqué par la honte

17quand j’entends les outrages ╵et les propos blessants

d’un ennemi vindicatif.

18Tout cela nous est arrivé ╵sans que nous t’ayons délaissé

et sans que nous ayons trahi ╵ton alliance avec nous.

19Nous n’avons pas renié ╵nos engagements envers toi,

nous n’avons pas quitté la voie ╵que tu nous as prescrite.

20Pourtant, tu nous as écrasés ╵dans le domaine des chacals44.20 Lieu désert et inhabité (voir Es 13.22 ; Jr 9.11).,

et tu nous as couverts ╵de ténèbres épaisses.

21Si nous avions délaissé notre Dieu,

si nous avions tendu les mains ╵vers un dieu étranger,

22Dieu ne l’aurait-il pas appris,

lui qui connaît tous les secrets ╵qui sont au fond des cœurs ?

23A cause de toi, chaque jour, ╵nous sommes massacrés

et l’on nous considère ╵comme étant des moutons ╵destinés à la boucherie44.23 Cité en Rm 8.36..

24Interviens donc, Seigneur ! ╵Pourquoi ne réagis-tu pas ?

Veuille te réveiller ! ╵Ne nous rejette pas toujours !

25Pourquoi te détourner ?

Pourquoi ignores-tu nos maux ╵et nos détresses ?

26Car nous voilà prostrés dans la poussière,

plaqués au sol.

27Agis, viens à notre aide !

Libère-nous dans ton amour !