Masalimo 43 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 43:1-5

Salimo 43

1Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

O Livro

Salmos 43:1-5

Salmo 43

1Faz-me justiça, ó Deus;

defende-me das acusações desta gente ímpia.

Livra-me do homem enganador e perverso.

2Pois tu, meu Deus, és o lugar onde me abrigo.

Porque me pões de lado?

Porque hei de viver assim triste,

com a opressão dos meus inimigos?

3Envia-me a tua luz e a tua verdade,

para que me guiem e me levem

à tua santa habitação, ao teu santo monte.

4Então chegar-me-ei ao altar de Deus,

do Deus que é a minha grande alegria.

Eu te louvarei com a minha harpa, meu Deus!

5Porque estás abatida, ó minha alma?

Porque estás perturbada?

Confia em Deus, pois ainda o louvarei.

Ele é a minha salvação! Ele é o meu Deus!