Masalimo 43 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 43:1-5

Salimo 43

1Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

Het Boek

Psalmen 43:1-5

1Zorgt U voor mijn recht, God,

en voert U mijn verdediging tegen een goddeloos volk,

laat mij niet in de handen van oneerlijke mensen vallen.

2U bent immers de God tot wie ik kan vluchten?

Waarom helpt U mij niet?

Waarom moet ik terneergeslagen rondlopen,

onderdrukt door mijn tegenstanders?

3Stuur uw licht en uw waarheid om mij te begeleiden.

Laten zij mij naar uw heiligdom en naar uw woningen brengen.

4Want dan kan ik weer naar uw altaar gaan,

naar U, die de God van mijn vreugde bent.

Ik wil U lofzingen met mijn citer.

U bent mijn God!

5Waarom ben ik toch zo onrustig en terneergeslagen?

Ik wil op God vertrouwen,

Hem wil ik lofprijzen,

want Hij is mijn bevrijder en mijn God!