Masalimo 42 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 42:1-11

BUKU LACHIWIRI

Masalimo 42–72

Salimo 42

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi,

kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.

2Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo.

Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?

3Misozi yanga yakhala chakudya changa

usana ndi usiku,

pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti,

“Mulungu wako ali kuti?”

4Zinthu izi ndimazikumbukira

pamene ndikukhuthula moyo wanga:

momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu,

kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu

ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko

pakati pa anthu a pa chikondwerero.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Yembekezera Mulungu,

pakuti ndidzamulambirabe,

Mpulumutsi wanga ndi 6Mulungu wanga.

Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga

kotero ndidzakumbukira Inu

kuchokera ku dziko la Yorodani,

ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.

7Madzi akuya akuyitana madzi akuya

mu mkokomo wa mathithi anu;

mafunde anu onse obwera mwamphamvu

andimiza.

8Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake,

nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane;

pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.

9Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa,

“Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?”

10Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo

pamene adani anga akundinyoza,

tsiku lonse akunena kuti,

“Mulungu wako ali kuti?”

11Bwanji ukumva chisoni,

iwe mtima wanga?

Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso,

Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

New Russian Translation

Псалтирь 42:1-5

Псалом 42

1Оправдай меня, Боже,

вступись в мою тяжбу с народом безбожным,

от лживых и злобных спаси меня.

2Ты – Бог, крепость моя.

Почему Ты отверг меня?

Почему я скитаюсь, плача,

оскорбленный моим врагом?

3Пошли Свой свет и истину –

пусть они меня направляют;

пусть приведут на святую гору Твою,

к месту, где Ты обитаешь.

4Тогда приду я к Божьему жертвеннику,

к Богу радости и веселья моего.

Буду славить Тебя на арфе,

Боже, мой Бог.

5Что унываешь, моя душа?

Зачем тревожишься?

Возложи надежду на Бога,

ведь я еще буду славить Его –

моего Спасителя и Бога.