Masalimo 42 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 42:1-11

BUKU LACHIWIRI

Masalimo 42–72

Salimo 42

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi,

kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.

2Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo.

Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?

3Misozi yanga yakhala chakudya changa

usana ndi usiku,

pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti,

“Mulungu wako ali kuti?”

4Zinthu izi ndimazikumbukira

pamene ndikukhuthula moyo wanga:

momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu,

kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu

ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko

pakati pa anthu a pa chikondwerero.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Yembekezera Mulungu,

pakuti ndidzamulambirabe,

Mpulumutsi wanga ndi 6Mulungu wanga.

Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga

kotero ndidzakumbukira Inu

kuchokera ku dziko la Yorodani,

ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.

7Madzi akuya akuyitana madzi akuya

mu mkokomo wa mathithi anu;

mafunde anu onse obwera mwamphamvu

andimiza.

8Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake,

nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane;

pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.

9Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa,

“Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?”

10Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo

pamene adani anga akundinyoza,

tsiku lonse akunena kuti,

“Mulungu wako ali kuti?”

11Bwanji ukumva chisoni,

iwe mtima wanga?

Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso,

Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

New International Version

Psalms 42:1-11

BOOK II

Psalms 42–72

Psalm 42In many Hebrew manuscripts Psalms 42 and 43 constitute one psalm.In Hebrew texts 42:1-11 is numbered 42:2-12.

For the director of music. A maskilTitle: Probably a literary or musical term of the Sons of Korah.

1As the deer pants for streams of water,

so my soul pants for you, my God.

2My soul thirsts for God, for the living God.

When can I go and meet with God?

3My tears have been my food

day and night,

while people say to me all day long,

“Where is your God?”

4These things I remember

as I pour out my soul:

how I used to go to the house of God

under the protection of the Mighty One42:4 See Septuagint and Syriac; the meaning of the Hebrew for this line is uncertain.

with shouts of joy and praise

among the festive throng.

5Why, my soul, are you downcast?

Why so disturbed within me?

Put your hope in God,

for I will yet praise him,

my Savior and my God.

6My soul is downcast within me;

therefore I will remember you

from the land of the Jordan,

the heights of Hermon—from Mount Mizar.

7Deep calls to deep

in the roar of your waterfalls;

all your waves and breakers

have swept over me.

8By day the Lord directs his love,

at night his song is with me—

a prayer to the God of my life.

9I say to God my Rock,

“Why have you forgotten me?

Why must I go about mourning,

oppressed by the enemy?”

10My bones suffer mortal agony

as my foes taunt me,

saying to me all day long,

“Where is your God?”

11Why, my soul, are you downcast?

Why so disturbed within me?

Put your hope in God,

for I will yet praise him,

my Savior and my God.