Masalimo 41 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 41:1-13

Salimo 41

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;

Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.

2Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;

Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko

ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.

3Yehova adzamuthandiza pamene akudwala

ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.

4Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;

chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”

5Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,

“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”

6Pamene wina abwera kudzandiona,

amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;

kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.

7Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,

iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,

8“Matenda owopsa amugwira;

sadzaukapo pamalo pamene wagona.”

9Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,

iye amene amadya pamodzi ndi ine

watukula chidendene chake kulimbana nane.

10Koma Yehova mundichititre chifundo,

dzutseni kuti ndiwabwezere.

11Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,

pakuti mdani wanga sandigonjetsa.

12Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga

ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.

13Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli

kuchokera muyaya mpaka muyaya.

Ameni ndi Ameni.

King James Version

Psalms 41:1-13

To the chief Musician, A Psalm of David.

1Blessed is he that considereth the poor: the LORD will deliver him in time of trouble.41.1 the poor: or, the weak, or, sick41.1 in time…: Heb. in the day of evil

2The LORD will preserve him, and keep him alive; and he shall be blessed upon the earth: and thou wilt not deliver him unto the will of his enemies.41.2 thou…: or, do not thou deliver

3The LORD will strengthen him upon the bed of languishing: thou wilt make all his bed in his sickness.41.3 make: Heb. turn

4I said, LORD, be merciful unto me: heal my soul; for I have sinned against thee.

5Mine enemies speak evil of me, When shall he die, and his name perish?

6And if he come to see me, he speaketh vanity: his heart gathereth iniquity to itself; when he goeth abroad, he telleth it.

7All that hate me whisper together against me: against me do they devise my hurt.41.7 my…: Heb. evil to me

8An evil disease, say they, cleaveth fast unto him: and now that he lieth he shall rise up no more.41.8 An…: Heb. A thing of Belial

9Yea, mine own familiar friend, in whom I trusted, which did eat of my bread, hath lifted up his heel against me.41.9 mine…: Heb. the man of my peace41.9 lifted…: Heb. magnified

10But thou, O LORD, be merciful unto me, and raise me up, that I may requite them.

11By this I know that thou favourest me, because mine enemy doth not triumph over me.

12And as for me, thou upholdest me in mine integrity, and settest me before thy face for ever.

13Blessed be the LORD God of Israel from everlasting, and to everlasting. Amen, and Amen.