Masalimo 40 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 40:1-17

Salimo 40

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mofatsa ndinadikira Yehova

Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.

2Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,

mʼthope ndi mʼchithaphwi;

Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe

ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.

3Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,

nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.

Ambiri adzaona,

nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

4Ndi wodala munthu

amakhulupirira Yehova;

amene sayembekezera kwa odzikuza,

kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.

5Zambiri, Yehova Mulungu wanga,

ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.

Zinthu zimene munazikonzera ife

palibe amene angathe kukuwerengerani.

Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,

zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

6Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,

koma makutu anga mwawatsekula;

zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo

Inu simunazipemphe.

7Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.

Mʼbuku mwalembedwa za ine.

8Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;

lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

9Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;

sinditseka milomo yanga

monga mukudziwa Inu Yehova.

10Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;

ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.

Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu

pa msonkhano waukulu.

11Musandichotsere chifundo chanu Yehova;

chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.

12Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;

machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.

Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,

ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13Pulumutseni Yehova;

Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.

14Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga

achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;

onse amene amakhumba chiwonongeko changa

abwezedwe mwamanyazi.

15Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”

abwerere akuchita manyazi.

16Koma iwo amene amafunafuna Inu

akondwere ndi kusangalala mwa Inu;

iwo amene amakonda chipulumutso chanu

nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;

Ambuye andiganizire.

Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;

Inu Mulungu wanga, musachedwe.

New International Reader’s Version

Psalm 40:1-17

Psalm 40

For the director of music. A psalm of David.

1I was patient while I waited for the Lord.

He turned to me and heard my cry for help.

2I was sliding down into the pit of death, and he pulled me out.

He brought me up out of the mud and dirt.

He set my feet on a rock.

He gave me a firm place to stand on.

3He gave me a new song to sing.

It is a hymn of praise to our God.

Many people will see and have respect for the Lord.

They will put their trust in him.

4Blessed is the person

who trusts in the Lord.

They don’t trust in proud people.

Those proud people worship statues of gods.

5Lord my God,

no one can compare with you.

You have done many wonderful things.

You have planned to do these things for us.

There are too many of them

for me to talk about.

6You didn’t want sacrifices and offerings.

You didn’t require burnt offerings and sin offerings.

You opened my ears so that I could hear you and obey you.

7Then I said, “Here I am.

It is written about me in the book.

8My God, I have come to do what you want.

Your law is in my heart.”

9I have told the whole community of those who worship you.

I have told them what you have done to save me.

Lord, you know

that I haven’t kept quiet.

10I haven’t kept to myself that what you did for me was right.

I have spoken about how faithful you were when you saved me.

I haven’t hidden your love and your faithfulness

from the whole community.

11Lord, don’t hold back your mercy from me.

May your love and faithfulness always keep me safe.

12There are more troubles all around me than I can count.

My sins have caught up with me, and I can’t see any longer.

My sins are more than the hairs of my head.

I have lost all hope.

13Lord, please save me.

Lord, come quickly to help me.

14Let all those who are trying to kill me be put to shame.

Let them lose their way.

Let all those who want to destroy me

be turned back in shame.

15Some people make fun of me.

Let them be shocked when their plans fail.

16But let all those who seek you

be joyful and glad because of what you have done.

Let those who count on you to save them always say,

“The Lord is great!”

17But I am poor and needy.

May the Lord be concerned about me.

You are the God who helps me and saves me.

You are my God, so don’t wait any longer.