Masalimo 4 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 4:1-8

Salimo 4

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide.

1Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu,

Inu Mulungu wa chilungamo changa.

Pumulitseni ku zowawa zanga;

chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.

2Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi?

Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza?

Sela.

3Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika;

Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.

4Kwiyani koma musachimwe;

pamene muli pa mabedi anu,

santhulani mitima yanu ndi kukhala chete.

Sela

5Perekani nsembe zolungama

ndipo dalirani Yehova.

6Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?”

Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.

7Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu

kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.

8Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere,

pakuti Inu nokha, Inu Yehova,

mumandisamalira bwino.

New Russian Translation

Псалтирь 4:1-9

Псалом 4

1Дирижеру хора. На струнных инструментах. Псалом Давида.

2Ответь мне, когда я взываю к Тебе,

Бог мой, оправдывающий меня.

Когда мне было тесно, Ты вывел меня на простор.

Помилуй меня и молитву мою услышь.

3Люди, как долго вы будете меня чернить?

Как долго будете любить пустое, искать ложь? Пауза

4Знайте, верного Господь Себе отделил.

Господь услышит, когда я к Нему воззову.

5Гневаясь, не грешите;

задумайтесь об этом на ложах ваших и успокойтесь! Пауза

6Приносите жертвы правды

и уповайте на Господа.

7Многие спрашивают: «Кто покажет нам благо?»

Да озарит нас свет лица Твоего, о Господь!

8Ты наполнил мое сердце радостью большей,

чем у тех, у кого зерно и вино в изобилии.

9Я лягу и с миром засну,

потому что, Господи, только Ты

даешь мне жить в безопасности.