Masalimo 4 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 4:1-8

Salimo 4

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide.

1Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu,

Inu Mulungu wa chilungamo changa.

Pumulitseni ku zowawa zanga;

chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.

2Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi?

Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza?

Sela.

3Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika;

Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.

4Kwiyani koma musachimwe;

pamene muli pa mabedi anu,

santhulani mitima yanu ndi kukhala chete.

Sela

5Perekani nsembe zolungama

ndipo dalirani Yehova.

6Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?”

Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.

7Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu

kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.

8Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere,

pakuti Inu nokha, Inu Yehova,

mumandisamalira bwino.

New International Reader’s Version

Psalm 4:1-8

Psalm 4

For the director of music. A psalm of David to be played on stringed instruments.

1My faithful God,

answer me when I call out to you.

Give me rest from my trouble.

Have mercy on me. Hear my prayer.

2How long will you people turn my glory into shame?

How long will you love what will certainly fail you?

How long will you pray to statues of gods?

3Remember that the Lord has set apart his faithful servant for himself.

The Lord hears me when I call out to him.

4Tremble and do not sin.

When you are in bed,

look deep down inside yourself and be silent.

5Offer to the Lord the sacrifices that godly people offer.

Trust in him.

6Lord, many are asking, “Who will make us successful?”

Lord, may you do good things for us.

7Fill my heart with joy

when the people have lots of grain and fresh wine.

8In peace I will lie down and sleep.

Lord, you alone keep me safe.