Masalimo 39 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”

New International Version – UK

Psalms 39:1-13

Psalm 39In Hebrew texts 39:1-13 is numbered 39:2-14.

For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.

1I said, ‘I will watch my ways

and keep my tongue from sin;

I will put a muzzle on my mouth

while in the presence of the wicked.’

2So I remained utterly silent,

not even saying anything good.

But my anguish increased;

3my heart grew hot within me.

While I meditated, the fire burned;

then I spoke with my tongue:

4‘Show me, Lord, my life’s end

and the number of my days;

let me know how fleeting my life is.

5You have made my days a mere handbreadth;

the span of my years is as nothing before you.

Everyone is but a breath,

even those who seem secure.39:5 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 11.

6‘Surely everyone goes around like a mere phantom;

in vain they rush about, heaping up wealth

without knowing whose it will finally be.

7‘But now, Lord, what do I look for?

My hope is in you.

8Save me from all my transgressions;

do not make me the scorn of fools.

9I was silent; I would not open my mouth,

for you are the one who has done this.

10Remove your scourge from me;

I am overcome by the blow of your hand.

11When you rebuke and discipline anyone for their sin,

you consume their wealth like a moth –

surely everyone is but a breath.

12‘Hear my prayer, Lord,

listen to my cry for help;

do not be deaf to my weeping.

I dwell with you as a foreigner,

a stranger, as all my ancestors were.

13Look away from me, that I may enjoy life again

before I depart and am no more.’