Masalimo 39 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”

Ketab El Hayat

مزمور 39:1-13

الْمَزْمُورُ التَّاسِعُ والثَّلاثُونَ

لِقَائِدِ الْمُنْشِدِينَ، مَزْمُورٌ لِدَاوُدَ

1قُلْتُ: «أَحْرِصُ عَلَى حُسْنِ الْمَسْلَكِ فَلَا يُخْطِئُ لِسَانِي الْقَوْلَ. سَأَكُمُّ فَمِي عَنِ الْكَلامِ مَادَامَ الشِّرِّيرُ أَمَامِي». 2صَمَتُّ صَمْتاً. أَمْسَكْتُ حَتَّى عَنِ الْخَيْرِ، فَثَارَ وَجَعِي. 3الْتَهَبَ قَلْبِي فِي دَاخِلِي، وَفِي تَأَمُّلِي اشْتَعَلَتْ فِيَّ النَّارُ، فَأَطْلَقْتُ لِسَانِي بِالْكَلامِ. 4يَا رَبُّ عَرِّفْنِي مَتَى تَكُونُ نِهَايَتِي، وَكَمْ تَطُولُ أَيَّامِي فَأُدْرِكَ أَنَّنِي إِنْسَانٌ زَائِلٌ. 5هُوَذَا قَدْ جَعَلْتَ حَيَاتِي قَصِيرَةً، وَعُمْرِي كَلَا شَيْءَ أَمَامَكَ. كُلُّ إِنْسَانٍ حَيٍّ لَيْسَ سِوَى نَفْخَةٍ! 6إِنَّمَا كَخَيَالٍ يَتَمَشَّى الإِنْسَانُ، فَعَبَثاً يُكَافِحُ النَّاسُ. يَجْمَعُ الْوَاحِدُ مِنْهُمْ ثَرْوَةً وَلَا يَدْرِي مَنْ يَرِثُهَا مِنْ بَعْدِهِ.

7وَالآنَ، فَأَيُّ شَيْءٍ أَنْتَظِرُ يَا رَبُّ؟ إِنَّمَا فِيكَ رَجَائِي. 8نَجِّنِي مِنْ جَمِيعِ مَعَاصِيَّ، وَلَا تَجْعَلْنِي عَاراً عِنْدَ الأَحْمَقِ. 9صَمَتُّ. لَا أَفْتَحُ فَمِي، لأَنَّكَ أَنْتَ فَعَلْتَ هَذَا. 10ارْفَعْ عَنِّي ضَرْبَتَكَ فَقَدْ فَنِيْتُ مِنْ صَفْعَةِ يَدِكَ. 11عِنْدَمَا تُؤَدِّبُ الإِنْسَانَ بِالتَّوْبِيخِ عَلَى الإِثْمِ، تُتْلِفُ بَهَاءَهُ إِتْلافَ الْعُثِّ. إِنَّمَا كُلُّ إِنْسَانٍ نَفْخَةٌ. 12يَا رَبُّ اسْمَعْ صَلاتِي. وَأَصْغِ إِلَى صُرَاخِي، وَلَا تَسْكُتْ أَمَامَ دُمُوعِي، لأَنِّي غَرِيبٌ عِنْدَكَ وَعَابِرُ سَبِيلٍ كَجَمِيعِ آبَائِي. 13حَوِّلْ غَضَبَكَ عَنِّي فَأَنْتَعِشَ، قَبْلَ أَنْ أَمُوتَ وَيَخْتَفِيَ أَثَرِي.