Masalimo 39 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 39:1-13

第 39 篇

受苦者的呼求

大卫的诗,交给乐长耶杜顿。

1我说:“我要谨言慎行,

免犯口舌之罪。

只要身边有恶人,

我就用嚼环勒住自己的口。”

2然而,我默不作声,

连好话也不出口时,

内心就更加痛苦。

3我心如火烧,越沉思越烦躁,

便开口呼求:

4“耶和华啊,求你让我知道我人生的终点和寿数,

明白人生何其短暂。

5你使我的生命转瞬即逝,

我的岁月在你眼中不到片刻。

人的生命不过是一丝气息,(细拉)

6人生不过是幻影,

劳碌奔波却一场空,

积蓄财富却不知谁来享用。

7主啊,如今我盼望什么呢?

你是我的盼望。

8求你救我脱离一切过犯,

不要让愚昧人嘲笑我。

9我默然不语,一言不发,

因为我受的责罚是出于你。

10求你不要再惩罚我,

你的责打使我几乎丧命。

11因为人犯罪,你管教他们,

使他们所爱的被吞噬,像被虫蛀。

世人不过是一丝气息。(细拉)

12“耶和华啊,

求你垂听我的祷告,

倾听我的呼求,

别对我的眼泪视若无睹。

因为我在你面前只是客旅,

是寄居的,

正如我的祖先。

13求你宽恕我,

好让我在离世之前能重展笑容。”