Masalimo 38 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 38:1-22

Salimo 38

Salimo la Davide. Kupempha.

1Yehova musandidzudzule mutapsa mtima

kapena kundilanga muli ndi ukali.

2Pakuti mivi yanu yandilasa,

ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.

3Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;

mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.

4Kulakwa kwanga kwandipsinja

ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.

5Mabala anga akuwola ndipo akununkha

chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.

6Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;

tsiku lonse ndimangolira.

7Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,

mulibe thanzi mʼthupi langa.

8Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;

ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.

9Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,

kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.

10Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;

ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.

11Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;

anansi anga akhala kutali nane.

12Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo,

oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga;

tsiku lonse amakonza zachinyengo.

13Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve,

monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;

14Ndakhala ngati munthu amene samva,

amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.

15Ndikudikira Inu Yehova;

mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.

16Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere

kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”

17Pakuti ndili pafupi kugwa,

ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.

18Ndikuvomereza mphulupulu zanga;

ndipo ndavutika ndi tchimo langa.

19Ambiri ndi adani anga amphamvu;

amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.

20Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino

amandinyoza pamene nditsatira zabwino.

21Inu Yehova, musanditaye;

musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.

22Bwerani msanga kudzandithandiza,

Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

New Russian Translation

Псалтирь 38:1-14

Псалом 38

1Дирижеру хора, Идутуну38:1 Ср. 1 Пар. 16:41, 42.. Псалом Давида.

2Я сказал: «Я буду следить за своими путями

и язык удерживать от греха,

буду обуздывать уста,

пока нечестивые предо мною».

3Но когда я был нем и безмолвен,

и даже о добром молчал,

усилилась моя скорбь,

4и сердце мое загорелось.

Пока я размышлял, вспыхнул огонь,

и тогда я сказал своими устами:

5«Покажи мне, Господи, кончину мою

и число моих дней скажи;

дай мне знать, сколь жизнь моя быстротечна.

6Да, Ты дал мне дней лишь на ширину ладони;

мой век как ничто пред Тобой.

Поистине, всякая жизнь – лишь пар. Пауза

7Поистине, всякий человек подобен тени:

напрасно он суетится,

копит, не зная, кому все это достанется.

8И теперь, Владыка, чего ожидать мне?

Надежда моя в Тебе.

9Избавь меня от всех моих беззаконий,

не предай безумцам на поругание.

10Я молчу; я не открываю уст,

потому что Ты это сделал.

11Отклони от меня удары Свои;

гибну я от ударов Твоей руки.

12Ты коришь и наказываешь людей за грех;

Ты губишь сокровища их, как губит моль.

Поистине, всякий смертный – лишь пар. Пауза

13Услышь молитву мою, Господи;

внемли моему крику о помощи;

не будь безмолвен к моим слезам.

Ведь я скиталец у Тебя,

чужеземец, как все мои предки.

14Отступи от меня, чтобы мне вновь улыбнуться,

прежде чем я уйду и меня не станет».