Masalimo 37 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 37:1-40

Salimo 37

Salimo la Davide.

1Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa

kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;

2pakuti monga udzu iwo adzafota msanga,

ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.

3Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino;

khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.

4Udzikondweretse wekha mwa Yehova

ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.

5Pereka njira yako kwa Yehova;

dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:

6Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha,

chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.

7Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa;

usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo,

pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.

8Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali,

usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.

9Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa,

koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.

10Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso;

ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.

11Koma ofatsa adzalandira dziko

ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.

12Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama

ndipo amawakukutira mano;

13koma Ambuye amaseka oyipa

pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.

14Oyipa amasolola lupanga

ndi kupinda uta

kugwetsa osauka ndi osowa,

kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.

15Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe,

ndipo mauta awo anathyoka.

16Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo

ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;

17pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka,

koma Yehova amasunga olungama.

18Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova,

ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.

19Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota;

mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.

20Koma oyipa adzawonongeka;

adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo,

iwo adzazimirira ngati utsi.

21Oyipa amabwereka ndipo sabweza

koma olungama amapereka mowolowamanja.

22Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko,

koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.

23Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu,

amakhazikitsa mayendedwe ake;

24ngakhale atapunthwa sadzagwa,

pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.

25Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba

koma sindinaonepo olungama akusiyidwa

kapena ana awo akupempha chakudya.

26Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu;

ana awo adzadalitsika.

27Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.

28Pakuti Yehova amakonda wolungama

ndipo sadzasiya okhulupirika ake.

Iwo adzatetezedwa kwamuyaya,

koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;

29olungama adzalandira dziko

ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.

30Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru,

ndipo lilime lake limayankhula zolungama.

31Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake;

mapazi ake saterereka.

32Oyipa amabisala kudikira olungama;

kufunafuna miyoyo yawoyo;

33koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo

kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.

34Khulupirira Yehova,

ndipo sunga njira yake;

Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako;

udzaona anthu oyipa akuwonongeka.

35Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo

akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.

36Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso;

ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.

37Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama;

udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.

38Koma anthu ochimwa adzawonongeka;

iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.

39Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova;

Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.

40Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa;

Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa,

pakuti amathawira kwa Iye.

La Bible du Semeur

Psaumes 37:1-40

Le témoignage de l’expérience37 Psaume alphabétique (cf. note 9.1).

1De David.

Ne t’irrite pas ╵contre les méchants !

Ne jalouse pas ╵ceux qui font le mal !

2Car, rapidement, ╵comme l’herbe aux champs, ╵ils seront fauchés

et se faneront ╵comme la verdure.

3Mets en l’Eternel ╵toute ta confiance ! ╵Fais ce qui est bien,

et, dans le pays, ╵tu demeureras ╵et tu jouiras ╵de bons pâturages ╵en sécurité.

4En Dieu, mets ta joie

et il comblera ╵les vœux de ton cœur.

5C’est à l’Eternel ╵qu’il te faut remettre ╵ta vie tout entière.

Aie confiance en lui ╵et il agira.

6Il fera paraître ╵ta justice ╵comme la lumière,

et ton droit ╵comme le soleil ╵à midi.

7Demeure en silence ╵devant l’Eternel. ╵Attends-toi à lui,

ne t’irrite pas ╵contre ceux qui réussissent ╵dans leurs entreprises,

en mettant en œuvre ╵de mauvais desseins.

8Laisse la colère, ╵calme ton courroux,

ne t’irrite pas, ╵car, en fin de compte, ╵tu ferais le mal.

9Or, qui fait le mal ╵sera retranché :

mais ceux qui comptent sur l’Eternel ╵auront le pays ╵comme possession.

10D’ici peu de temps, ╵fini le méchant !

Tu auras beau le chercher : ╵il ne sera plus.

11Mais ceux qui sont humbles37.11 Autre traduction : doux. ╵auront le pays ╵comme possession37.11 Cité enMt 5.5.,

et ils jouiront ╵d’une grande paix.

12Le méchant complote ╵pour faire du tort au juste,

il grince des dents ╵contre lui.

13Pourtant l’Eternel ╵se moque de lui,

car il voit venir ╵le jour de sa perte.

14Les méchants tirent l’épée,

ils bandent leur arc

pour tuer le pauvre ╵et le défavorisé

et pour égorger ╵tous les gens qui suivent ╵la voie droite.

15Mais leur propre épée ╵leur transpercera le cœur,

et quant à leurs arcs, ╵ils seront brisés.

16Le peu que possède ╵celui qui est juste

vaut bien mieux que la richesse ╵de nombreux méchants.

17Les méchants verront ╵leur pouvoir brisé,

mais l’Eternel reste ╵le soutien des justes.

18L’Eternel tient compte ╵de ce qu’est la vie ╵des gens sans reproche37.18 Autre traduction : L’Eternel veille sur chacun des jours des gens sans reproche.,

et leur patrimoine ╵demeure à jamais.

19Pour eux, pas de honte ╵au temps du malheur,

et, dans les jours de famine ╵ils auront de quoi se rassasier.

20Les méchants périssent

et les ennemis de l’Eternel ╵sont comme les fleurs des prés :

ils disparaîtront ; ╵comme une fumée, ╵ils s’évanouiront.

21Le méchant emprunte ╵mais il ne rend pas ;

le juste a pitié, ╵il est généreux.

22Ceux que Dieu bénit ╵auront le pays ╵comme possession37.22 Voir note v. 11.,

mais ceux qu’il maudit ╵seront retranchés.

23Lorsque la conduite ╵de quelqu’un lui plaît,

l’Eternel lui donne ╵d’affermir sa marche ╵dans la vie.

24Il peut trébucher, ╵mais il ne s’écroule pas :

l’Eternel le tient ╵par la main.

25Depuis ma jeunesse ╵jusqu’à mon âge avancé,

jamais je n’ai vu ╵celui qui est juste ╵être abandonné,

ni ses descendants ╵mendier leur pain.

26Tout au long des jours, ╵il a compassion ╵et il prête aux autres.

Ses enfants seront ╵en bénédiction.

27Evite le mal, ╵accomplis le bien :

tu demeureras ╵pour toujours.

28Car l’Eternel aime la droiture,

et il n’abandonne pas ╵ceux qui lui sont attachés ;

mais les malfaisants ╵seront supprimés37.28 mais les malfaisants seront supprimés: d’après l’ancienne version grecque, qui suppose la disparition d’un mot et la confusion entre deux lettres très ressemblantes par rapport au texte hébreu traditionnel qui porte : ils seront gardés éternellement. D’une part, la leçon de la version grecque permet de préserver le parallélisme entre les deux dernières lignes du verset. D’autre part, le terme manquant dans l’hébreu est nécessaire à la construction de l’acrostiche du psaume.,

la postérité ╵de tous les méchants ╵sera retranchée ;

29tandis que les justes ╵auront le pays ╵comme possession.

Ils l’habiteront ╵éternellement.

30Des paroles sages ╵sortent de la bouche ╵de ceux qui sont justes,

et leur langue parle, ╵selon la droiture.

31Ils ont dans leur cœur ╵la Loi de leur Dieu,

et ils ne trébuchent pas.

32Le méchant épie le juste :

il cherche à le mettre à mort.

33L’Eternel ╵ne le livre pas en son pouvoir.

Il ne le laissera pas ╵être condamné ╵dans un jugement.

34Attends-toi à l’Eternel, ╵règle ta conduite ╵selon ce qu’il a prescrit :

il t’honorera ╵par la possession ╵du pays.

Tu verras comment ╵tous les malfaisants ╵seront retranchés.

35J’ai vu le méchant, ╵dans sa violence,

croître comme un arbre florissant ╵bien enraciné ╵sur son sol natal.

36Puis je suis passé par là37.36 D’après un manuscrit de Qumrân et les version anciennes. Texte hébreu traditionnel : il a passé. : ╵voici qu’il n’est plus.

Et j’ai eu beau le chercher, ╵il est introuvable.

37Considère l’homme intègre,

oui, observe l’homme droit :

alors tu constateras ╵que l’homme de paix ╵a un avenir.

38Au contraire les rebelles ╵seront détruits tous ensemble,

et les méchants n’auront plus ╵aucun avenir.

39Le salut des justes ╵vient de l’Eternel,

et il est leur forteresse ╵aux jours de détresse.

40Il leur vient en aide ╵et il les délivre ;

il les fait échapper aux méchants ╵et les sauve

car ils ont cherché ╵leur refuge en lui.