Masalimo 35 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 35:1-28

Salimo 35

Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;

mumenyane nawo amene akumenyana nane.

2Tengani chishango ndi lihawo;

dzukani ndipo bwerani mundithandize.

3Tengani mkondo ndi nthungo,

kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.

Uzani moyo wanga kuti,

“Ine ndine chipulumutso chako.”

4Iwo amene akufunafuna moyo wanga

anyozedwe ndi kuchita manyazi;

iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke

abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.

5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo

pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.

6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera

pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.

7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa

ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,

8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa

ukonde umene iwo abisa uwakole,

agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.

9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova

ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.

10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,

“Ndani angafanane nanu Yehova?

Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,

osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,

zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.

12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino

ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.

13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli

ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.

Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,

14ndinayendayenda ndi kulira maliro,

kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.

Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima

kukhala ngati ndikulira amayi anga.

15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;

ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.

Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.

16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;

anandikukutira mano awo.

17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?

Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,

moyo wanga wopambana ku mikango.

18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19Musalole adani anga onyenga

akondwere chifukwa cha masautso anga;

musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa

andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.

20Iwowo sayankhula mwamtendere,

koma amaganizira zonamizira

iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.

21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!

Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.

Ambuye musakhale kutali ndi ine.

23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!

Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.

24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.

Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.

25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”

Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26Onse amene amakondwera ndi masautso anga

achite manyazi ndi kusokonezeka.

Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,

avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.

27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,

afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.

Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,

Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”

28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu

ndi za matamando anu tsiku lonse.

Het Boek

Psalmen 35:1-28

1Een lied van David.

Here, als sommigen met mij argumenteren,

wilt U dan voor mij antwoorden?

Als iemand mij aanvalt,

vecht U dan voor mij terug.

2Neem uw wapens op

en kom mij te hulp!

3Val mijn achtervolgers aan.

Laat mij weten dat U mij zult verlossen!

4Laat hen die mij willen doden,

voor schut staan.

Laat hen die slechte plannen tegen mij beramen,

beschaamd afdruipen.

5Verstrooi hen als kaf in de wind,

op het moment dat uw Engel hen neerslaat.

6Zij gaan op donkere, glibberige wegen

en de Engel van de Here achtervolgt hen daarop.

7Want zonder aanleiding spanden zij een net voor mij

en groeven een valkuil om mij te vangen.

8Ik hoop dat zij zonder het te merken zelf omkomen.

Dat zij in hun eigen kuil zullen vallen.

9Ik verheug mij in de Here,

ik zing een loflied over zijn hulp en bevrijding.

10Alles in mij juicht:

Here, wie kan U evenaren?

U bevrijdt arme en beproefde mensen

van hun onderdrukkers en berovers.

11Leugenachtige getuigen nemen het woord

en vragen mij dingen die ik helemaal niet weet.

12Zij vergelden goed met kwaad.

Mijn ziel is eenzaam geworden.

13Zelf heb ik mij direct in rouwkleding gestoken

toen zij ziek waren.

Ik vernederde mij voor U met vasten

wanneer mijn gebed niet verhoord werd.

14Ik liep rond alsof het mijn broer of mijn vriend betrof,

ik ging in het zwart alsof mijn moeder was gestorven.

15Maar toen ík een keer in problemen zat,

lachten zij om mij en liepen te hoop om mij te zien.

Zelfs onbekenden begonnen mij te slaan

en maakten mij onophoudelijk bespottelijk.

16Een heel stel ongelovige, spotlustige lieden

bedreigde mij.

17Here,

hoe lang laat U hen nog hun gang gaan?

Verlos mij toch, ik ben eenzaam.

Laten zij mij niet verslinden.

18Dan zal ik U te midden van alle gelovigen loven,

U prijzen waar iedereen bij is.

19Laten mijn valse tegenstanders toch geen plezier over mij hebben!

Er zijn er die mij zonder reden haten!

20Zij zijn niet op vrede uit.

Zij maken slechte plannen,

gericht tegen hen die in rust en stilte leven.

21Zij bedreigen mij en zeggen:

‘Ha! Wij hebben het wel gezien!’

22U ziet alles, Here, wilt U optreden?

Och Here, laat mij niet in de steek!

23Sta op en vecht voor mijn recht.

God, mijn Here, voert U voor mij het woord in de rechtzaal.

24Laat uw recht over mij beslissen, Here, mijn God,

zodat zij geen leedvermaak over mij kunnen hebben.

25Dat zij niet kunnen denken:

‘Ha! Nu gebeurt wat wij willen!

Wij hebben hem eronder gekregen!’

26Laten zij zich maar schamen,

al die mensen die op mijn ondergang zitten te wachten.

Ik hoop dat allen die mij verachten, te schande worden gemaakt.

27Maar ik wil dat alle mensen

die verlangen naar mijn vrijspraak,

zullen juichen en zich verheugen.

Dat zij voortdurend de Here zullen grootmaken en zeggen:

‘De Here trekt Zich het lot van zijn geliefde dienaar aan.’

28Zelf zal ik dag in, dag uit

over uw rechtvaardigheid spreken

en U loven en prijzen.