Masalimo 35 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 35:1-28

Salimo 35

Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;

mumenyane nawo amene akumenyana nane.

2Tengani chishango ndi lihawo;

dzukani ndipo bwerani mundithandize.

3Tengani mkondo ndi nthungo,

kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.

Uzani moyo wanga kuti,

“Ine ndine chipulumutso chako.”

4Iwo amene akufunafuna moyo wanga

anyozedwe ndi kuchita manyazi;

iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke

abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.

5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo

pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.

6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera

pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.

7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa

ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,

8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa

ukonde umene iwo abisa uwakole,

agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.

9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova

ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.

10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,

“Ndani angafanane nanu Yehova?

Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,

osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,

zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.

12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino

ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.

13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli

ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.

Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,

14ndinayendayenda ndi kulira maliro,

kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.

Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima

kukhala ngati ndikulira amayi anga.

15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;

ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.

Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.

16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;

anandikukutira mano awo.

17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?

Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,

moyo wanga wopambana ku mikango.

18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19Musalole adani anga onyenga

akondwere chifukwa cha masautso anga;

musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa

andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.

20Iwowo sayankhula mwamtendere,

koma amaganizira zonamizira

iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.

21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!

Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.

Ambuye musakhale kutali ndi ine.

23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!

Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.

24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.

Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.

25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”

Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26Onse amene amakondwera ndi masautso anga

achite manyazi ndi kusokonezeka.

Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,

avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.

27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,

afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.

Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,

Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”

28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu

ndi za matamando anu tsiku lonse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 35:1-28

第 35 篇

求上帝伸冤

大衛的詩。

1耶和華啊,

求你與我的敵人為敵,

攻擊那些攻擊我的人。

2求你拿起大小盾牌來幫助我,

3舉起矛槍攻擊追趕我的人。

求你對我說:

「我是你的拯救。」

4願謀殺我的人蒙羞受辱,

謀害我的人落荒而逃!

5願耶和華的天使驅散他們,

如風吹散糠秕!

6願他們的道路漆黑泥濘,

有耶和華的天使在後追趕!

7因為他們無故設網羅,

挖陷阱要害我。

8願他們突遭禍患,

作繭自縛,自食惡果!

9我要因耶和華而歡欣,

因祂的拯救而快樂。

10我從心底發出讚歎:

耶和華啊,誰能像你?

你拯救弱者免受欺壓,

拯救窮人免遭掠奪。

11惡人誣告我,

盤問我毫無所知的事情。

12他們對我以惡報善,

令我傷心欲絕。

13他們生病時,

我披上麻衣,

謙卑地為他們禁食禱告,

但上帝沒有垂聽。

14我為他們哀傷,

視他們為朋友、弟兄;

我低頭為他們哭泣,

如同哀悼自己的母親。

15我遭遇患難時,

他們卻聚在一起幸災樂禍,

合夥誹謗我。

素不相識的人也群起攻擊我,

不住地譭謗我。

16他們肆無忌憚地嘲弄我,

咬牙切齒地憎惡我。

17耶和華啊,

你袖手旁觀要到何時?

求你救我的性命免遭殘害,

救我脫離這些獅子。

18我要在大會中稱謝你,

在眾人面前讚美你。

19求你不要讓無故攻擊我的人幸災樂禍,

不要讓無故恨我的人沾沾自喜。

20他們言語暴戾,

謀害安分守己的人。

21他們高喊:「哈哈!哈哈!

我們親眼看見了。」

22耶和華啊,這一切你都看見了,

求你不要再緘默,不要遠離我。

23我的上帝,我的主啊,

求你起來為我辯護,為我伸冤。

24我的上帝耶和華啊,

求你按你的公義宣告我無罪,

別讓他們幸災樂禍。

25別讓他們說:

「哈哈,我們如願以償了!」

別讓他們說:

「我們除掉他了!」

26願幸災樂禍的人蒙羞受辱,

自高自大的人無地自容!

27願盼望我冤屈得雪的人揚聲歡呼!

願他們常說:「耶和華當受尊崇!

祂樂意賜福給自己的僕人。」

28我要訴說你的公義,

終日讚美你。