Masalimo 35 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 35:1-28

Salimo 35

Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;

mumenyane nawo amene akumenyana nane.

2Tengani chishango ndi lihawo;

dzukani ndipo bwerani mundithandize.

3Tengani mkondo ndi nthungo,

kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.

Uzani moyo wanga kuti,

“Ine ndine chipulumutso chako.”

4Iwo amene akufunafuna moyo wanga

anyozedwe ndi kuchita manyazi;

iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke

abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.

5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo

pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.

6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera

pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.

7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa

ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,

8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa

ukonde umene iwo abisa uwakole,

agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.

9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova

ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.

10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,

“Ndani angafanane nanu Yehova?

Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,

osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,

zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.

12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino

ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.

13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli

ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.

Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,

14ndinayendayenda ndi kulira maliro,

kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.

Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima

kukhala ngati ndikulira amayi anga.

15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;

ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.

Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.

16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;

anandikukutira mano awo.

17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?

Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,

moyo wanga wopambana ku mikango.

18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19Musalole adani anga onyenga

akondwere chifukwa cha masautso anga;

musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa

andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.

20Iwowo sayankhula mwamtendere,

koma amaganizira zonamizira

iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.

21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!

Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.

Ambuye musakhale kutali ndi ine.

23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!

Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.

24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.

Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.

25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”

Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26Onse amene amakondwera ndi masautso anga

achite manyazi ndi kusokonezeka.

Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,

avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.

27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,

afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.

Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,

Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”

28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu

ndi za matamando anu tsiku lonse.

La Bible du Semeur

Psaumes 35:1-28

Le Seigneur protège les faibles

1De David.

O Eternel, viens accuser ╵ceux qui m’accusent,

combats toi-même ╵qui me combat.

2Saisis le petit bouclier ╵et le grand bouclier,

lève-toi pour me secourir !

3Brandis ta lance ╵avec le javelot ╵contre mes poursuivants !

Dis-moi que tu es mon Sauveur.

4Qu’ils soient honteux, déshonorés, ╵ceux qui en veulent à ma vie !

Qu’ils reculent couverts d’opprobre, ╵ceux qui projettent mon malheur !

5Qu’ils soient comme la paille ╵emportée par le vent,

quand les repoussera ╵l’ange de l’Eternel35.5 Voir note 34.8. !

6Que leur chemin soit sombre, ╵qu’il soit glissant

lorsque l’ange de l’Eternel ╵viendra les pourchasser !

7Sans cause, ils ont caché ╵des pièges sur ma route,

sans raison, pour me perdre, ╵ils ont creusé des fosses.

8Que le malheur s’abatte ╵sur eux à l’improviste !

Et que dans le filet ╵qu’ils ont caché, ╵ils puissent s’empêtrer !

Qu’ils tombent dans la fosse ╵qu’ils ont creusée ╵et qu’elle fasse ╵leur propre ruine35.8 La version syriaque a : qu’ils ont creusée pour moi..

9J’exulterai de joie ╵en l’Eternel,

je me réjouirai ╵pour le salut ╵qu’il aura accompli pour moi.

10Je clamerai de tout mon être : ╵« Eternel, qui est comme toi ?

Le malheureux, tu le délivres ╵d’un ennemi plus fort que lui,

les pauvres et les démunis, ╵tu les libères ╵de ceux qui les oppriment. »

11Des témoins adonnés à la violence se lèvent,

on vient m’interroger ╵sur des faits que j’ignore.

12Ils me rendent le mal ╵pour le bien que j’ai fait.

Je suis abandonné.

13Et moi, quand ils étaient malades, ╵je revêtais un vêtement de deuil

et je m’humiliais en jeûnant.

Sans cesse, je priais pour eux35.13 Autre traduction : quand ma prière n’était pas exaucée.

14comme pour un ami ╵ou pour un frère. ╵J’allais, courbé sous la tristesse,

comme en menant le deuil ╵pour la mort d’une mère.

15Je suis tombé dans le malheur : ╵les voilà qui s’attroupent ╵en triomphant à mon sujet ;

oui, ils s’attroupent contre moi ╵pour m’attaquer à mon insu35.15 à mon insu: autre traduction : ces gens que je ne connais pas..

Sans répit, ils m’outragent.

16Avec une ironie mordante, ╵ces hypocrites

grincent des dents à mon sujet.

17Seigneur, comment ╵supportes-tu cela ?

Soustrais ma vie à leurs sévices,

ma vie qui m’est précieuse, ╵à ces lions !

18Je te rendrai hommage ╵dans la grande assemblée.

Je te louerai ╵avec la foule immense.

19Sans cause, ils sont mes ennemis : ╵qu’ils ne triomphent pas ╵à mon sujet !

Ils me détestent sans raison. ╵Qu’ils n’osent plus cligner de l’œil ╵pour m’insulter !

20Car ce n’est pas la paix ╵qu’apporte leur parole,

ils forgent des mensonges ╵contre les gens paisibles du pays.

21La bouche grande ouverte,

ils disent : ╵« Eh, eh ! Nous l’avons vu ! »

22Eternel, toi, tu as tout vu ! ╵Ne reste pas muet !

Seigneur, ne te tiens pas ╵si éloigné de moi !

23Interviens donc !

Oui, interviens ╵pour défendre mon droit,

toi, mon Dieu, mon Seigneur, ╵pour prendre en main ma cause !

24Rends-moi justice, ╵toi qui es juste, ╵ô Eternel mon Dieu !

Empêche-les ╵de triompher à mon sujet !

25Qu’ils ne se disent pas : ╵« Ah, ah, c’est ce que nous voulions ! »

Non, qu’ils ne disent pas : ╵« Nous n’avons fait de lui ╵qu’une bouchée ! »

26Que la honte et le déshonneur ╵atteignent tous ceux qui se réjouissent ╵de mon malheur !

Qu’ils soient couverts de honte ╵et revêtus de confusion,

ceux qui, pour se grandir, ╵se tournent contre moi !

27Alors ceux qui désirent ╵voir mon droit rétabli

pourront se réjouir, ╵et ils crieront de joie

en répétant sans cesse : ╵« Que l’Eternel est grand,

lui qui désire ╵le bonheur de son serviteur ! »

28Oui, je proclamerai que tu es juste,

je dirai ta louange tout le jour.