Masalimo 34 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 34:1-22

Salimo 34

Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.

1Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;

matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.

2Moyo wanga udzanyadira Yehova;

anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.

3Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;

tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

4Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;

anandilanditsa ku mantha anga onse.

5Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;

nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.

6Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;

Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.

7Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye

ndi kuwalanditsa.

8Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;

wodala munthu amene amathawira kwa Iye.

9Wopani Yehova inu oyera mtima ake,

pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.

10Mikango itha kulefuka ndi kumva njala

koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.

11Bwerani ana anga, mundimvere;

ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.

12Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake

ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,

13asunge lilime lake ku zoyipa

ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.

14Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

funafuna mtendere ndi kuwulondola.

15Maso a Yehova ali pa olungama

ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;

16nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,

kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.

17Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;

Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.

18Yehova ali pafupi kwa osweka mtima

ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.

19Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,

Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,

20Iye amateteza mafupa ake onse,

palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.

21Choyipa chidzapha anthu oyipa;

adani a olungama adzapezeka olakwa.

22Yehova amawombola atumiki ake;

aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 34:1-23

Fordelen ved at adlyde Gud

1En sang af David om dengang, han foregav at være gået fra forstanden foran kong Abimelek, så kongen sendte ham væk.

2Jeg vil prise Herren til hver en tid,

altid fortælle om hans magt og storhed.

3Jeg glæder mig over, hvad Herren har gjort,

lad de forkuede høre det og fryde sig.

4Kom og slut jer til mig,

lad os sammen prise Herren.

5Jeg bad Herren om hjælp, og han svarede mig,

han befriede mig fra al min frygt.

6De, som stoler på Herren, skal stråle af glæde,

for han vil aldrig nogensinde skuffe dem.

7Jeg råbte til Herren i min nød,

og han reddede mig ud af mine problemer.

8For Herrens engel redder enhver,

som ønsker at gøre Guds vilje.

9Prøv selv at opleve Herrens godhed,

lykkelige er de, der søger hjælp hos ham.

10Adlyd Herren, I, som tilhører ham,

de, der følger ham, får, hvad de har brug for.

11Selv stærke løver lider nød og sulter,

men de, der stoler på Herren, lider ingen nød.

12Kom, mine børn, og hør, hvad jeg siger.

Jeg vil lære jer, hvordan man viser Herren ære.

13I, der gerne vil have et godt liv

og ønsker jer gode dage,

14I skal holde jeres tunge i skak

og ikke lade løgn komme over jeres læber.

15Hold jer fra det onde,

gør det gode og stræb efter fred.

16Herren beskytter de retskafne

og hører deres bøn om hjælp.

17Men han er imod dem, der handler ondt.

Han udrydder dem helt, så de ikke huskes.

18Han hører de retsindiges råb om hjælp,

redder dem ud af deres problemer.

19Herren er hos dem, der føler sig knust,

han hjælper dem, der er dybt deprimerede.

20De uskyldige kommer også ud i problemer,

men Herren hjælper dem igennem dem alle.

21Ja, han beskytter dem fra alt det onde,

så de ikke bliver knust derved.

22De onde må bøde for deres ondskab,

de, der bekæmper de uskyldige, bliver straffet.

23Men Herren redder sine tjenere.

De, der søger ham, bliver ikke straffet.