Masalimo 33 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 33:1-22

Salimo 33

1Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,

nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.

2Mutamandeni Yehova ndi pangwe;

muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.

3Muyimbireni nyimbo yatsopano;

imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.

4Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;

Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.

5Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;

dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.

6Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,

zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.

7Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;

amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.

8Dziko lonse lapansi liope Yehova;

anthu onse amulemekeze Iye.

9Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;

Iye analamulira ndipo zinakhazikika.

10Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;

Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.

11Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,

zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.

12Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,

anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.

13Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi

ndi kuona anthu onse;

14kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira

onse amene amakhala pa dziko lapansi.

15Iye amene amapanga mitima ya onse,

amaona zonse zimene akuchita.

16Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;

palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.

17Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,

ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.

18Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,

19kuwawombola iwo ku imfa

ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.

20Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.

21Mwa Iye mitima yathu imakondwera,

pakuti ife timadalira dzina lake loyera.

22Chikondi chanu chosatha

chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

Nueva Versión Internacional

Salmo 33:1-22

Salmo 33

1Canten al Señor con alegría, ustedes los justos;

es propio de los íntegros alabar al Señor.

2Alaben al Señor al son del arpa;

entonen alabanzas con la lira de diez cuerdas.

3Cántenle una canción nueva;

toquen con destreza

y den voces de alegría.

4La palabra del Señor es justa;

fieles son todas sus obras.

5El Señor ama la justicia y el derecho;

llena está la tierra de su gran amor.

6Por la palabra del Señor fueron hechos los cielos

y por el soplo de su boca, todo lo que en ellos hay.

7Él recoge en cántaros las aguas del mar

y junta en depósitos las profundidades del océano.

8Que toda la tierra tema al Señor;

que lo honren todos los pueblos del mundo;

9porque él habló, todo fue hecho;

dio una orden y todo quedó firme.

10El Señor frustra los planes de las naciones;

desbarata los designios de los pueblos.

11Pero los planes del Señor quedan firmes para siempre;

los designios de su corazón son eternos.

12Dichosa la nación cuyo Dios es el Señor,

el pueblo que escogió por su heredad.

13El Señor observa desde el cielo

y ve a toda la humanidad;

14él contempla desde su morada

a todos los habitantes de la tierra.

15Él es quien formó el corazón de todos

y quien conoce a fondo todas sus acciones.

16No se salva el rey por sus muchos soldados

ni por su mucha fuerza se libra el valiente.

17Vana esperanza de victoria es el caballo;

a pesar de su mucha fuerza no puede salvar.

18Los ojos del Señor están sobre los que le temen;

de los que esperan en su gran amor.

19Él los libra de la muerte

y en épocas de hambre los mantiene con vida.

20Esperamos confiados en el Señor;

él es nuestro socorro y nuestro escudo.

21En él se regocija nuestro corazón,

porque confiamos en su santo nombre.

22Que tu gran amor, Señor, nos acompañe,

tal como lo esperamos de ti.