Masalimo 33 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 33:1-22

Salimo 33

1Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,

nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.

2Mutamandeni Yehova ndi pangwe;

muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.

3Muyimbireni nyimbo yatsopano;

imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.

4Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;

Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.

5Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;

dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.

6Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,

zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.

7Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;

amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.

8Dziko lonse lapansi liope Yehova;

anthu onse amulemekeze Iye.

9Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;

Iye analamulira ndipo zinakhazikika.

10Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;

Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.

11Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,

zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.

12Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,

anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.

13Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi

ndi kuona anthu onse;

14kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira

onse amene amakhala pa dziko lapansi.

15Iye amene amapanga mitima ya onse,

amaona zonse zimene akuchita.

16Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;

palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.

17Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,

ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.

18Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,

19kuwawombola iwo ku imfa

ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.

20Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.

21Mwa Iye mitima yathu imakondwera,

pakuti ife timadalira dzina lake loyera.

22Chikondi chanu chosatha

chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

Nova Versão Internacional

Salmos 33:1-22

Salmo 33

1Cantem de alegria ao Senhor, vocês que são justos;

aos que são retos fica bem louvá-lo.

2Louvem o Senhor com harpa;

ofereçam-lhe música com lira de dez cordas.

3Cantem-lhe uma nova canção;

toquem com habilidade ao aclamá-lo.

4Pois a palavra do Senhor é verdadeira;

ele é fiel em tudo o que faz.

5Ele ama a justiça e a retidão;

a terra está cheia da bondade do Senhor.

6Mediante a palavra do Senhor foram feitos os céus,

e os corpos celestes, pelo sopro de sua boca.

7Ele ajunta as águas do mar num só lugar;

das profundezas faz reservatórios.

8Toda a terra tema o Senhor;

tremam diante dele todos os habitantes do mundo.

9Pois ele falou, e tudo se fez;

ele ordenou, e tudo surgiu.

10O Senhor desfaz os planos das nações

e frustra os propósitos dos povos.

11Mas os planos do Senhor permanecem para sempre,

os propósitos do seu coração, por todas as gerações.

12Como é feliz a nação que tem o Senhor como Deus,

o povo que ele escolheu para lhe pertencer!

13Dos céus olha o Senhor

e vê toda a humanidade;

14do seu trono ele observa

todos os habitantes da terra;

15ele, que forma o coração de todos,

que conhece tudo o que fazem.

16Nenhum rei se salva pelo tamanho do seu exército;

nenhum guerreiro escapa por sua grande força.

17O cavalo é vã esperança de vitória;

apesar da sua grande força, é incapaz de salvar.

18Mas o Senhor protege aqueles que o temem,

aqueles que firmam a esperança no seu amor,

19para livrá-los da morte e garantir-lhes vida,

mesmo em tempos de fome.

20Nossa esperança está no Senhor;

ele é o nosso auxílio e a nossa proteção.

21Nele se alegra o nosso coração,

pois confiamos no seu santo nome.

22Esteja sobre nós o teu amor, Senhor,

como está em ti a nossa esperança.