Masalimo 33 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 33:1-22

Salimo 33

1Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,

nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.

2Mutamandeni Yehova ndi pangwe;

muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.

3Muyimbireni nyimbo yatsopano;

imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.

4Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;

Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.

5Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;

dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.

6Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,

zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.

7Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;

amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.

8Dziko lonse lapansi liope Yehova;

anthu onse amulemekeze Iye.

9Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;

Iye analamulira ndipo zinakhazikika.

10Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;

Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.

11Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,

zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.

12Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,

anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.

13Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi

ndi kuona anthu onse;

14kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira

onse amene amakhala pa dziko lapansi.

15Iye amene amapanga mitima ya onse,

amaona zonse zimene akuchita.

16Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;

palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.

17Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,

ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.

18Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,

19kuwawombola iwo ku imfa

ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.

20Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.

21Mwa Iye mitima yathu imakondwera,

pakuti ife timadalira dzina lake loyera.

22Chikondi chanu chosatha

chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 33:1-22

第 33 篇

颂赞之歌

1义人啊,

你们要欢然歌颂耶和华,

正直的人理应赞美祂。

2你们要弹琴赞美耶和华,

弹奏十弦琴赞美祂。

3要为祂唱新歌,

琴声要美妙,歌声要嘹亮。

4因为耶和华的话是真理,

祂的作为信实可靠。

5祂喜爱公平正义,

大地充满祂的慈爱。

6诸天靠祂的话而造,

群星靠祂口中的气而成。

7祂将海水聚在一处,把汪洋收进仓库。

8愿普世都敬畏耶和华!

愿世人都尊崇祂!

9因为祂一发话,就创造了天地;

祂一命令,就立定了万物。

10祂挫败列国的谋算,

拦阻列邦的计划。

11祂的计划永不落空,

祂的旨意万代长存。

12尊祂为上帝的邦国有福了!

蒙拣选做祂子民的人有福了!

13祂从天上俯视人间,

14从祂的居所察看世上万民。

15祂塑造人心,

洞察人的一切行为。

16君王不能靠兵多取胜,

勇士不能凭力大获救。

17靠战马取胜实属妄想,

马虽力大也不能救人。

18但耶和华看顾敬畏祂、仰望祂慈爱的人。

19祂救他们脱离死亡,

保护他们度过饥荒。

20我们仰望耶和华,

祂是我们的帮助,

是我们的盾牌。

21我们信靠祂的圣名,

我们的心因祂而充满喜乐。

22耶和华啊,我们仰望你,求你向我们施慈爱。