Masalimo 33 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 33:1-22

Salimo 33

1Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,

nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.

2Mutamandeni Yehova ndi pangwe;

muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.

3Muyimbireni nyimbo yatsopano;

imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.

4Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;

Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.

5Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;

dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.

6Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,

zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.

7Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;

amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.

8Dziko lonse lapansi liope Yehova;

anthu onse amulemekeze Iye.

9Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;

Iye analamulira ndipo zinakhazikika.

10Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;

Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.

11Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,

zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.

12Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,

anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.

13Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi

ndi kuona anthu onse;

14kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira

onse amene amakhala pa dziko lapansi.

15Iye amene amapanga mitima ya onse,

amaona zonse zimene akuchita.

16Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;

palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.

17Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,

ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.

18Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,

19kuwawombola iwo ku imfa

ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.

20Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.

21Mwa Iye mitima yathu imakondwera,

pakuti ife timadalira dzina lake loyera.

22Chikondi chanu chosatha

chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

Священное Писание

Забур 33:1-23

Песнь 33Песнь 33 В оригинале эта песнь написана в форме акростиха: каждый стих начинается с очередной буквы еврейского алфавита.

1Песнь Давуда, когда он притворялся безумным перед Ави-Маликом, был изгнан от него и удалился33:1 Ср. 1 Цар. 21:10–22:1..

2Буду славить Вечного во всякое время;

хвала Ему всегда на устах моих.

3Душа моя будет хвалиться Вечным;

пусть услышат кроткие и возвеселятся.

4Славьте со мною Вечного;

превознесём Его имя вместе!

5Я искал Вечного, и Он мне ответил

и от всех моих страхов меня избавил.

6Кто обращал к Нему взор, сияет от радости;

лица их не покроет стыд.

7Этот бедняк воззвал, и Вечный услышал его

и от всех напастей избавил его.

8Ангел Вечного33:8 Ангел Вечного – этот особенный ангел отождествляется с Самим Вечным. Многие толкователи видят в Нём явления Исы Масиха до Его воплощения. То же в 35:5, 6. встаёт на защиту вокруг боящихся Вечного,

и избавляет их.

9Вкусите и увидите, как благ Вечный!

Благословен тот, кто уповает на Него.

10Святой народ, бойся Вечного,

ведь тот, кто боится Его, ни в чём не нуждается.

11Бывает, что даже молодые львы бедствуют и голодают,

а ищущие Вечного не имеют нужды ни в каком благе.

12Придите, дети, послушайте меня;

я научу вас страху перед Вечным.

13Кто хочет радоваться жизни

и желает увидеть много добрых дней,

14пусть удержит свой язык от зла

и свои уста от коварных речей.

15Удаляйся от зла и твори добро;

ищи мира и стремись к нему.

16Глаза Вечного обращены на праведных,

и уши Его открыты для их мольбы,

17но гнев Вечного на тех, кто делает зло,

чтобы истребить память о них на земле.

18Взывают праведные, и Вечный их слышит

и от всех скорбей их избавляет.

19Близок Вечный к сокрушённым сердцем,

Он спасает смиренных духом.

20Много скорбей у праведного,

но от всех их избавляет его Вечный.

21Он все его кости хранит,

ни одна из них не будет переломлена33:21 Эти слова также являются пророчеством об Исе Масихе (см. Ин. 19:32, 33, 36)..

22Зло погубит нечестивого;

ненавидящие праведного будут осуждены.

23Вечный спасает жизнь Своих рабов,

и никто из надеющихся на Него не будет осуждён.