Masalimo 32 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 32:1-11

Salimo 32

Salimo la Davide. Malangizo.

1Ngodala munthu

amene zolakwa zake zakhululukidwa;

amene machimo ake aphimbidwa.

2Ngodala munthu

amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye

ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.

3Pamene ndinali chete,

mafupa anga anakalamba

chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.

4Pakuti usana ndi usiku

dzanja lanu linandipsinja;

mphamvu zanga zinatha

monga nthawi yotentha yachilimwe.

Sela

5Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu,

sindinabise mphulupulu zanga.

Ndinati, “Ine ndidzawulula

zolakwa zanga kwa Yehova,

ndipo Inu munandikhululukira

mlandu wa machimo anga.”

Sela

6Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo

pomwe mukupezeka;

ndithu pamene madzi amphamvu auka,

sadzamupeza.

7Inu ndi malo anga obisala;

muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga

ndi nyimbo zachipulumutso.

Sela

8Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo;

ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.

9Usakhale ngati kavalo kapena bulu,

zimene zilibe nzeru,

koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu,

ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.

10Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa

koma chikondi chosatha cha Yehova

chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.

11Kondwerani mwa Yehova inu olungama;

imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!