Masalimo 32 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 32:1-11

Salimo 32

Salimo la Davide. Malangizo.

1Ngodala munthu

amene zolakwa zake zakhululukidwa;

amene machimo ake aphimbidwa.

2Ngodala munthu

amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye

ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.

3Pamene ndinali chete,

mafupa anga anakalamba

chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.

4Pakuti usana ndi usiku

dzanja lanu linandipsinja;

mphamvu zanga zinatha

monga nthawi yotentha yachilimwe.

Sela

5Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu,

sindinabise mphulupulu zanga.

Ndinati, “Ine ndidzawulula

zolakwa zanga kwa Yehova,

ndipo Inu munandikhululukira

mlandu wa machimo anga.”

Sela

6Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo

pomwe mukupezeka;

ndithu pamene madzi amphamvu auka,

sadzamupeza.

7Inu ndi malo anga obisala;

muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga

ndi nyimbo zachipulumutso.

Sela

8Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo;

ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.

9Usakhale ngati kavalo kapena bulu,

zimene zilibe nzeru,

koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu,

ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.

10Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa

koma chikondi chosatha cha Yehova

chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.

11Kondwerani mwa Yehova inu olungama;

imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

Het Boek

Psalmen 32:1-11

1Een leerzaam gedicht van David.

Gelukkig is hij wiens misstap vergeven wordt

en wiens zonden vergeten worden.

2Gelukkig is hij

aan wie de Here zijn zonde niet toerekent

en wiens innerlijk eerlijk en oprecht is.

3Zolang ik mijn zonde niet beleed,

kwijnde ik weg.

Ik was de hele dag tot tranen toe bewogen.

4Dag en nacht voelde ik

hoe U tot mijn geweten sprak.

Ik schrompelde in elkaar als bij grote hitte.

5Toen heb ik U al mijn zonden beleden

en niets voor U verborgen gehouden.

Ik zei: ‘Ik zal de Here alles opbiechten’

en toen hebt U mijn schuld vergeven.

6Laat iedere gelovige veel tot U bidden,

nu U Zich nog laat vinden.

Zelfs al komt grote ellende op hem af,

dan nog zult U hem beschermen.

7U verbergt mij.

U spaart mij voor moeilijke omstandigheden.

U vult mijn hart met lofliederen over mijn bevrijding.

8‘Ik, de Here, laat u zien

welke weg u moet gaan.

Ik geef u raad

en houd mijn oog op u gericht.

9Gedraag u dus niet als een paard of een muildier,

dat met bit en teugels in bedwang moet worden gehouden.

Dat wil Ik niet.’

10Iemand die zonder God leeft,

krijgt veel zorgen en moeite te verduren.

Maar wie op de Here vertrouwt,

wordt door zijn liefde en goedheid omringd.

11Wees blij in de Here en zing een loflied, alle gelovigen!

Laten allen die oprecht tegenover God staan het uitjubelen.