Masalimo 31 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

New International Reader’s Version

Psalm 31:1-24

Psalm 31

For the director of music. A psalm of David.

1Lord, I have come to you for safety.

Don’t let me ever be put to shame.

Save me, because you do what is right.

2Pay attention to me.

Come quickly to help me.

Be the rock I go to for safety.

Be the strong fort that saves me.

3You are my rock and my fort.

Lead me and guide me for the honor of your name.

4Keep me free from the trap that is set for me.

You are my place of safety.

5Into your hands I commit my very life.

Lord, set me free. You are my faithful God.

6I hate those who worship worthless statues of gods.

But I trust in the Lord.

7I will be glad and full of joy because you love me.

You saw that I was hurting.

You took note of my great pain.

8You have not handed me over to the enemy.

You have put me in a wide and safe place.

9Lord, have mercy on me. I’m in deep trouble.

I’m so sad I can hardly see.

My whole body grows weak with sadness.

10Pain has taken over my life.

My years are spent in groaning.

I have no strength because I’m hurting so much.

My body is getting weaker and weaker.

11My neighbors make fun of me

because I have so many enemies.

My closest friends are afraid of me.

People who see me on the street run away from me.

12No one remembers me. I might as well be dead.

I have become like broken pottery.

13I hear many people whispering,

“There is terror all around him!”

Many have joined together against me.

They plan to kill me.

14But I trust in you, Lord.

I say, “You are my God.”

15My whole life is in your hands.

Save me from the hands of my enemies.

Save me from those who are chasing me.

16May you look on me with favor.

Save me because your love is faithful.

17Lord, I have cried out to you.

Don’t let me be put to shame.

But let sinners be put to shame.

Let them lie silent in the place of the dead.

18Their lips tell lies. Let them be silenced.

They speak with pride against those who do right.

They make fun of them.

19You have stored up so many good things.

You have stored them up for those who have respect for you.

You give those things while everyone watches.

You give them to people who run to you for safety.

20They are safe because you are with them.

You hide them from the evil plans of their enemies.

In your house you keep them safe

from those who bring charges against them.

21Give praise to the Lord.

He showed me his wonderful love

when my enemies attacked the city I was in.

22I was afraid and said,

“I’ve been cut off from you!”

But you heard my cry for your favor.

You heard me when I called out to you for help.

23Love the Lord, all you who are faithful to him!

The Lord keeps safe those who are faithful to him.

But he completely pays back those who are proud.

24Be strong, all you who put your hope in the Lord.

Never give up.