Masalimo 31 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 31:1-24

第 31 篇

信靠上帝的禱告

大衛的詩,交給樂長。

1耶和華啊,我尋求你的庇護,

求你讓我永不蒙羞;

你是公義的,求你拯救我。

2求你側耳聽我的呼求,

快來救我,作我堅固的避難所,

作拯救我的堡壘。

3你是我的磐石,我的堡壘,

求你為了自己的名而引導我,帶領我。

4你是我的避難所,

求你救我脫離人們為我設下的陷阱。

5我將靈魂交托給你。

信實的上帝耶和華啊,

你必救贖我。

6我憎恨拜假神的人,

我信靠耶和華。

7你已經看見我的困苦,

知道我心中的愁煩,

你的恩慈使我歡喜快樂。

8你沒有將我交給仇敵,

而是領我到寬闊之地。

9耶和華啊,我落在苦難之中,

求你憐憫我,

我雙眼哭腫,身心疲憊。

10我的生命被愁苦吞噬,

歲月被哀傷耗盡,

力量因罪惡而消逝,

我成了枯骨一堆。

11仇敵羞辱我,

鄰居厭棄我,

朋友害怕我,

路人紛紛躲避我。

12我就像已死之人,被人遺忘;

又像破碎的陶器,被人丟棄。

13我聽見許多人譭謗我,

驚恐籠罩著我。

他們圖謀不軌,

謀害我的性命。

14然而,耶和華啊,

我依然信靠你;

我說:「你是我的上帝。」

15我的時日都掌握在你手中,

求你救我脫離仇敵和追逼我的人。

16求你笑顏垂顧僕人,

施慈愛拯救我。

17耶和華啊,我曾向你呼求,

求你不要叫我蒙羞。

求你使惡人蒙羞,

寂然無聲地躺在陰間。

18願你堵住撒謊之人的口,

他們驕傲自大,

狂妄地攻擊義人。

19你的恩惠何其大——為敬畏你的人而預備,

在世人面前賜給投靠你的人。

20你把他們藏在你那裡,

使他們得到庇護,

免遭世人暗算。

你使他們在你的居所安然無恙,

免受惡言惡語的攻擊。

21耶和華當受稱頌!

因為我被困城中時,

祂以奇妙的愛待我。

22我曾驚恐地說:

「你丟棄了我!」

其實你聽了我的呼求。

23耶和華忠心的子民啊,

你們要愛祂。

祂保護忠心的人,

嚴懲驕傲的人。

24凡仰望耶和華的人啊,

要剛強壯膽!