Masalimo 3 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 3:1-8

Salimo 3

Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu.

1Inu Yehova, achulukadi adani anga!

Achulukadi amene andiwukira!

2Ambiri akunena za ine kuti,

“Mulungu sadzamupulumutsa.”

Sela

3Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza,

Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.

4Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula

ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera.

Sela

5Ine ndimagona ndi kupeza tulo;

ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.

6Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene

abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.

7Dzukani, Inu Yehova!

Pulumutseni, Inu Mulungu wanga.

Akantheni adani anga onse pa msagwada;

gululani mano a anthu oyipa.

8Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.

Madalitso akhale pa anthu anu.

Sela

New International Version

Psalms 3:1-8

Psalm 3In Hebrew texts 3:1-8 is numbered 3:2-9.

A psalm of David. When he fled from his son Absalom.

1Lord, how many are my foes!

How many rise up against me!

2Many are saying of me,

“God will not deliver him.”3:2 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 4 and 8.

3But you, Lord, are a shield around me,

my glory, the One who lifts my head high.

4I call out to the Lord,

and he answers me from his holy mountain.

5I lie down and sleep;

I wake again, because the Lord sustains me.

6I will not fear though tens of thousands

assail me on every side.

7Arise, Lord!

Deliver me, my God!

Strike all my enemies on the jaw;

break the teeth of the wicked.

8From the Lord comes deliverance.

May your blessing be on your people.