Masalimo 29 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 29:1-11

Salimo 29

Salimo la Davide.

1Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,

pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

3Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;

Mulungu waulemerero abangula,

Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.

4Liwu la Yehova ndi lamphamvu;

liwu la Yehova ndi laulemerero.

5Liwu la Yehova limathyola mikungudza;

Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.

6Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,

Siriyoni ngati mwana wa njati:

7Liwu la Yehova limakantha

ngati kungʼanima kwa mphenzi.

8Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;

Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.

9Liwu la Yehova limapindapinda mibawa

ndi kuyeretsa nkhalango.

Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

10Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,

Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.

11Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;

Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

King James Version

Psalms 29:1-11

A Psalm of David.

1Give unto the LORD, O ye mighty, give unto the LORD glory and strength.29.1 ye mighty: Heb. ye sons of the mighty

2Give unto the LORD the glory due unto his name; worship the LORD in the beauty of holiness.29.2 the glory…: Heb. the honour of his name29.2 in…: or, in his glorious sanctuary

3The voice of the LORD is upon the waters: the God of glory thundereth: the LORD is upon many waters.29.3 many: or, great

4The voice of the LORD is powerful; the voice of the LORD is full of majesty.29.4 powerful: Heb. in power29.4 full…: Heb. in majesty

5The voice of the LORD breaketh the cedars; yea, the LORD breaketh the cedars of Lebanon.

6He maketh them also to skip like a calf; Lebanon and Sirion like a young unicorn.

7The voice of the LORD divideth the flames of fire.29.7 divideth: Heb. cutteth out

8The voice of the LORD shaketh the wilderness; the LORD shaketh the wilderness of Kadesh.

9The voice of the LORD maketh the hinds to calve, and discovereth the forests: and in his temple doth every one speak of his glory.29.9 to calve: or, to be in pain29.9 doth…: or, every whit of it uttereth, etc

10The LORD sitteth upon the flood; yea, the LORD sitteth King for ever.

11The LORD will give strength unto his people; the LORD will bless his people with peace.