Masalimo 28 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

New International Version

Psalms 28:1-9

Psalm 28

Of David.

1To you, Lord, I call;

you are my Rock,

do not turn a deaf ear to me.

For if you remain silent,

I will be like those who go down to the pit.

2Hear my cry for mercy

as I call to you for help,

as I lift up my hands

toward your Most Holy Place.

3Do not drag me away with the wicked,

with those who do evil,

who speak cordially with their neighbors

but harbor malice in their hearts.

4Repay them for their deeds

and for their evil work;

repay them for what their hands have done

and bring back on them what they deserve.

5Because they have no regard for the deeds of the Lord

and what his hands have done,

he will tear them down

and never build them up again.

6Praise be to the Lord,

for he has heard my cry for mercy.

7The Lord is my strength and my shield;

my heart trusts in him, and he helps me.

My heart leaps for joy,

and with my song I praise him.

8The Lord is the strength of his people,

a fortress of salvation for his anointed one.

9Save your people and bless your inheritance;

be their shepherd and carry them forever.