Masalimo 28 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

Japanese Contemporary Bible

詩篇 28:1-9

28

1ああ主よ、どうかお助けください。

あなたは安全を守る私の岩です。

あなたに顔をそむけられたら、

いっさいをあきらめ、死ぬしかありません。

2主よ。私は両手を差し伸べ、

主が助けてくださることをひたすら願っているのです。

どうか、私の叫びを聞いてください。

3隣人に愛想をふりまきながら、

心の中ではひそかに相手を殺そうと企む

悪者どもといっしょに、私を罰しないでください。

4彼らに見合う罰が下りますように。

その悪事の大きさにしたがって罰を重くし、

すべてのしわざに報いてください。

5彼らは神のことになど無関心で、

神が何をなさろうとおかまいなしです。

ですから、古い建物のように神の手で取りこわされ、

二度と建て直されません。

6訴えを取り上げてくださった主をほめたたえます。

7主は私の力、あらゆる危険から身を守る盾です。

私の信頼に答えて、神は助けてくださいました。

心にわき上がる喜びは、賛美の歌となってあふれます。

8神はご自分の民を守り、

油を注がれた王に勝利をもたらしてくださいます。

9主よ、あなたの民を守ってください。

主に選ばれた者を守り、祝福してください。

羊飼いとなって、いつまでも彼らを

抱きかかえて運んでください。