Masalimo 27 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 27:1-14

Salimo 27

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?

Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

2Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane

kudzadya mnofu wanga,

pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,

iwo adzapunthwa ndi kugwa.

3Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,

mtima wanga sudzaopa.

Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,

ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,

ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:

kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova

masiku onse a moyo wanga,

ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,

ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.

5Pakuti pa tsiku la msautso

Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;

adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake

ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.

6Kotero mutu wanga udzakwezedwa

kuposa adani anga amene andizungulira;

pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;

ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

7Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova

mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.

8Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”

Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.

9Musandibisire nkhope yanu,

musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;

mwakhala muli thandizo langa.

Musandikane kapena kunditaya,

Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.

10Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya

Yehova adzandisamala.

11Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,

munditsogolere mʼnjira yowongoka

chifukwa cha ondizunza.

12Musandipereke ku zokhumba za adani anga,

pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane

ndipo zikundiopseza.

13Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;

ndidzaona ubwino wa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

14Dikirani pa Yehova;

khalani anyonga ndipo limbani mtima

nimudikire Yehova.

King James Version

Psalms 27:1-14

A Psalm of David.

1The LORD is my light and my salvation; whom shall I fear? the LORD is the strength of my life; of whom shall I be afraid?

2When the wicked, even mine enemies and my foes, came upon me to eat up my flesh, they stumbled and fell.27.2 came…: Heb. approached against me

3Though an host should encamp against me, my heart shall not fear: though war should rise against me, in this will I be confident.

4One thing have I desired of the LORD, that will I seek after; that I may dwell in the house of the LORD all the days of my life, to behold the beauty of the LORD, and to enquire in his temple.27.4 the beauty: or, the delight

5For in the time of trouble he shall hide me in his pavilion: in the secret of his tabernacle shall he hide me; he shall set me up upon a rock.

6And now shall mine head be lifted up above mine enemies round about me: therefore will I offer in his tabernacle sacrifices of joy; I will sing, yea, I will sing praises unto the LORD.27.6 joy: Heb. shouting

7Hear, O LORD, when I cry with my voice: have mercy also upon me, and answer me.

8When thou saidst, Seek ye my face; my heart said unto thee, Thy face, LORD, will I seek.27.8 When…: or, My heart said unto thee, Let my face seek thy face, etc

9Hide not thy face far from me; put not thy servant away in anger: thou hast been my help; leave me not, neither forsake me, O God of my salvation.

10When my father and my mother forsake me, then the LORD will take me up.27.10 take…: Heb. gather me

11Teach me thy way, O LORD, and lead me in a plain path, because of mine enemies.27.11 a plain…: Heb. a way of plainness27.11 mine…: Heb. those which observe me

12Deliver me not over unto the will of mine enemies: for false witnesses are risen up against me, and such as breathe out cruelty.

13I had fainted, unless I had believed to see the goodness of the LORD in the land of the living.

14Wait on the LORD: be of good courage, and he shall strengthen thine heart: wait, I say, on the LORD.