Masalimo 27 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 27:1-14

Salimo 27

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?

Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

2Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane

kudzadya mnofu wanga,

pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,

iwo adzapunthwa ndi kugwa.

3Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,

mtima wanga sudzaopa.

Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,

ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,

ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:

kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova

masiku onse a moyo wanga,

ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,

ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.

5Pakuti pa tsiku la msautso

Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;

adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake

ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.

6Kotero mutu wanga udzakwezedwa

kuposa adani anga amene andizungulira;

pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;

ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

7Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova

mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.

8Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”

Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.

9Musandibisire nkhope yanu,

musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;

mwakhala muli thandizo langa.

Musandikane kapena kunditaya,

Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.

10Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya

Yehova adzandisamala.

11Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,

munditsogolere mʼnjira yowongoka

chifukwa cha ondizunza.

12Musandipereke ku zokhumba za adani anga,

pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane

ndipo zikundiopseza.

13Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;

ndidzaona ubwino wa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

14Dikirani pa Yehova;

khalani anyonga ndipo limbani mtima

nimudikire Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 27:1-14

Tillid til Herren

1En sang af David.

Herren er mit lys og min redning,

så hvem har jeg grund til at frygte?

Herren beskytter mit liv,

hvad har jeg så at være bange for?

2Når mine fjender angriber mig og vil mig til livs,

så snubler de alle og falder.

3Selv om jeg omringes af en hær, er jeg ikke bange.

Selv om alt tyder på krig, er jeg stadig tryg.

4Jeg har bedt Herren om én ting,

og det er mit højeste ønske:

at få lov at leve i hans nærhed livet igennem,

at se hans herlighed og meditere i hans helligdom.

5Herren beskytter mig,

når der er fare på færde.

Han skjuler mig i sit telt,

sætter mig højt på en klippe.

6Dér kan jeg være i fred,

for fjenden kan ikke nå mig.

Dér vil jeg bringe ofre til Herren

og lovprise ham af hele mit hjerte.

7Herre, hør min bøn!

Vær mig nådig og svar mig.

8Mit hjerte byder mig at søge dig,

og derfor kommer jeg til dig.27,8 Teksten er uklar.

9Vend mig ikke ryggen, Herre.

Vis ikke din tjener bort i vrede.

Du er min redning, svigt mig ikke nu!

Lad mig ikke i stikken, min frelses Gud!

10Selv hvis min far og mor forlod mig,

ville du altid blive hos mig, Herre.

11Vis mig den vej, jeg bør følge,

led mig på ærlighedens sti.

Mine fjender venter på, at jeg falder.

12Lad mig ikke falde i hænderne på dem!

De anklager mig for ting, jeg ikke har gjort,

og de er altid ude på vold.

13Men jeg er sikker på, at Herren vil hjælpe mig,

så jeg oplever hans godhed hele mit liv.

14Regn med Herren og hold ud!

Stol på ham og tab ikke modet!