Masalimo 27 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 27:1-14

Salimo 27

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?

Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

2Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane

kudzadya mnofu wanga,

pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,

iwo adzapunthwa ndi kugwa.

3Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,

mtima wanga sudzaopa.

Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,

ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,

ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:

kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova

masiku onse a moyo wanga,

ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,

ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.

5Pakuti pa tsiku la msautso

Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;

adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake

ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.

6Kotero mutu wanga udzakwezedwa

kuposa adani anga amene andizungulira;

pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;

ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

7Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova

mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.

8Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”

Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.

9Musandibisire nkhope yanu,

musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;

mwakhala muli thandizo langa.

Musandikane kapena kunditaya,

Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.

10Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya

Yehova adzandisamala.

11Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,

munditsogolere mʼnjira yowongoka

chifukwa cha ondizunza.

12Musandipereke ku zokhumba za adani anga,

pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane

ndipo zikundiopseza.

13Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;

ndidzaona ubwino wa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

14Dikirani pa Yehova;

khalani anyonga ndipo limbani mtima

nimudikire Yehova.

La Bible du Semeur

Psaumes 27:1-14

En sécurité auprès de Dieu

1De David.

Oui, l’Eternel est ma lumière ╵et mon Sauveur :

de qui aurais-je crainte ?

L’Eternel est ma forteresse : ╵il protège ma vie ;

de qui aurais-je peur ?

2Que des méchants ╵s’avancent contre moi,

voulant me nuire,

ce sont mes ennemis, ╵mes oppresseurs,

qui perdent pied et tombent.

3Qu’une armée vienne m’assiéger,

mon cœur reste sans crainte.

Que l’on me déclare la guerre,

je suis plein d’assurance.

4J’ai présenté à l’Eternel ╵un seul souhait, ╵mais qui me tient vraiment à cœur :

je voudrais habiter ╵dans la maison de l’Eternel ╵tous les jours de ma vie

afin d’admirer l’Eternel ╵dans sa beauté27.4 Autre traduction : dans sa douceur.,

et de chercher à le connaître27.4 Autre traduction : pour l’interroger. ╵dans sa demeure.

5Car il me cache sous sa tente ╵dans les jours du malheur.

Au secret de son tabernacle, ╵il me tient abrité ;

sur un rocher, ╵il me met hors d’atteinte.

6Dès à présent, ╵je peux lever la tête ╵pour dominer ╵mes ennemis autour de moi.

J’offrirai dans son tabernacle ╵des sacrifices ╵avec des cris de joie,

je célébrerai l’Eternel ╵par le chant et les instruments.

7O Eternel, ╵écoute mon appel ╵car je t’invoque.

Accorde-moi la grâce ╵de me répondre.

8Du fond de mon cœur, je me dis, ╵de ta part : « Tournez-vous vers moi ! »

Oui, c’est vers toi que je me tourne, ╵ô Eternel,

9ne te détourne pas de moi

et ne repousse pas ╵ton serviteur avec colère !

Toi qui m’as secouru,

ne me délaisse pas ! ╵Ne m’abandonne pas,

ô Dieu, toi qui es mon Sauveur !

10Si mon père et ma mère ╵devaient m’abandonner,

l’Eternel me recueillerait.

11Enseigne-moi la voie ╵que tu veux que je suive, ╵ô Eternel,

et conduis-moi ╵par un sentier égal,

puisque mes ennemis me guettent.

12Ne m’abandonne pas ╵aux désirs de mes adversaires

lorsque de faux témoins ╵se dressent contre moi,

respirant la violence.

13Que deviendrais-je ╵si je n’avais pas l’assurance ╵d’expérimenter la bonté ╵de l’Eternel

au pays des vivants ?

14Attends-toi donc à l’Eternel !

Sois fort ! ╵Affermis ton courage !

Oui, attends-toi à l’Eternel !