Salimo 26
Salimo la Davide.
1Weruzeni Inu Yehova
pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
popanda kugwedezeka.
2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
7kulengeza mofuwula za matamando anu
ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
malo amene ulemerero wanu umapezekako.
9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
12Ndayima pa malo wopanda zovuta
ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Salmo 26
Salmo de David.
1Senhor, faz-me justiça,
pois tenho andado com integridade.
Sempre tenho confiado em ti,
por isso, não hesitarei nem recuarei.
2Examina-me, Senhor,
e confirma que é assim mesmo;
observa bem o meu íntimo, os meus sentimentos.
3Porque penso muito na tua bondade;
a tua verdade é a lei da minha vida.
4Não convivo com gente falsa nem hipócrita.
5Detesto ajuntamentos de malfeitores;
não me chego aos que te desprezam.
6Lavo as mãos em sinal da minha inocência
e para poder prestar-te culto diante do teu altar.
7Para poder cantar-te publicamente louvores,
contando, assim, as tuas maravilhas.
8Senhor, eu amo a tua morada
e o lugar em que está a tua gloriosa habitação.
9Não deixes nunca que eu fique
em igualdade de circunstâncias com os pecadores.
Não deixes que a minha vida fique associada
à conduta de homens sanguinários,
10Nas suas mãos só há assassínios;
nada fazem sem subornos.
11Quanto a mim, procuro andar em integridade;
livra-me e tem compaixão de mim.
12Os meus pés andam num caminho plano.
Louvarei o Senhor publicamente.