Salimo 26
Salimo la Davide.
1Weruzeni Inu Yehova
pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
popanda kugwedezeka.
2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
7kulengeza mofuwula za matamando anu
ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
malo amene ulemerero wanu umapezekako.
9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
12Ndayima pa malo wopanda zovuta
ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Psalm 26
Of David.
1Vindicate me, Lord,
for I have led a blameless life;
I have trusted in the Lord
and have not faltered.
2Test me, Lord, and try me,
examine my heart and my mind;
3for I have always been mindful of your unfailing love
and have lived in reliance on your faithfulness.
4I do not sit with the deceitful,
nor do I associate with hypocrites.
5I abhor the assembly of evildoers
and refuse to sit with the wicked.
6I wash my hands in innocence,
and go about your altar, Lord,
7proclaiming aloud your praise
and telling of all your wonderful deeds.
8Lord, I love the house where you live,
the place where your glory dwells.
9Do not take away my soul along with sinners,
my life with those who are bloodthirsty,
10in whose hands are wicked schemes,
whose right hands are full of bribes.
11I lead a blameless life;
deliver me and be merciful to me.
12My feet stand on level ground;
in the great congregation I will praise the Lord.