Masalimo 26 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 26:1-12

Salimo 26

Salimo la Davide.

1Weruzeni Inu Yehova

pakuti ndakhala moyo wosalakwa.

Ndadalira Yehova

popanda kugwedezeka.

2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,

santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;

3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,

ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.

4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,

kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.

5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa

ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.

6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga

ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,

7kulengeza mofuwula za matamando anu

ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.

8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,

malo amene ulemerero wanu umapezekako.

9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,

moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,

10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,

dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.

11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;

mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.

12Ndayima pa malo wopanda zovuta

ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.