Salimo 26
Salimo la Davide.
1Weruzeni Inu Yehova
pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
popanda kugwedezeka.
2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
7kulengeza mofuwula za matamando anu
ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
malo amene ulemerero wanu umapezekako.
9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
12Ndayima pa malo wopanda zovuta
ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
선한 사람의 기도
(다윗의 시)
1여호와여,
내가 흠 없이 살고
흔들림이 없이
주를 의지하였습니다.
나에게 죄가 없음을 인정해 주소서.
2여호와여,
나를 살피시고 시험하셔서
내 마음의 생각과
동기를 알아보소서.
3주의 한결같은 사랑이
언제나 내 앞에 있으므로
내가 주의 진리 가운데 걸어갑니다.
4내가 거짓된 자들과
자리를 같이하지 않고
위선자들과 사귀지도 않습니다.
5나는 악을 행하는 자들과
어울리는 것을 싫어하며
그들과 함께 앉지도 않습니다.
6여호와여,
내가 무죄함을 보이려고 손을 씻고
주의 제단 앞에 나아가
7감사의 찬송을 부르며
주의 놀라운 일을 말합니다.
8여호와여, 주가 계신 집과
주의 영광이 있는 곳을
내가 사랑합니다.
9나의 영혼을 죄인들과 함께,
나의 생명을 살인자들과 함께
거두어 가지 마소서.
10그들은 언제나 악을 행하며
뇌물을 받기에 급급하지만
11나는 흠 없이 살아가고 있습니다.
여호와여, 나를 불쌍히 여기시고
구해 주소서.
12내가 모든 위험 가운데서도
넘어지지 않고 안전하게 섰으니
많은 사람 앞에서
여호와를 찬양하겠습니다.