Salimo 26
Salimo la Davide.
1Weruzeni Inu Yehova
pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
popanda kugwedezeka.
2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
7kulengeza mofuwula za matamando anu
ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
malo amene ulemerero wanu umapezekako.
9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
12Ndayima pa malo wopanda zovuta
ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
A Psalm of David.
1Judge me, O LORD; for I have walked in mine integrity: I have trusted also in the LORD; therefore I shall not slide.
2Examine me, O LORD, and prove me; try my reins and my heart.
3For thy lovingkindness is before mine eyes: and I have walked in thy truth.
4I have not sat with vain persons, neither will I go in with dissemblers.
5I have hated the congregation of evil doers; and will not sit with the wicked.
6I will wash mine hands in innocency: so will I compass thine altar, O LORD:
7That I may publish with the voice of thanksgiving, and tell of all thy wondrous works.
8LORD, I have loved the habitation of thy house, and the place where thine honour dwelleth.26.8 where…: Heb. of the tabernacle of thy honour
9Gather not my soul with sinners, nor my life with bloody men:26.9 Gather…: or, Take not away26.9 bloody…: Heb. men of blood
10In whose hands is mischief, and their right hand is full of bribes.26.10 full…: Heb. filled with
11But as for me, I will walk in mine integrity: redeem me, and be merciful unto me.
12My foot standeth in an even place: in the congregations will I bless the LORD.