Masalimo 26 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 26:1-12

Salimo 26

Salimo la Davide.

1Weruzeni Inu Yehova

pakuti ndakhala moyo wosalakwa.

Ndadalira Yehova

popanda kugwedezeka.

2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,

santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;

3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,

ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.

4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,

kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.

5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa

ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.

6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga

ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,

7kulengeza mofuwula za matamando anu

ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.

8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,

malo amene ulemerero wanu umapezekako.

9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,

moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,

10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,

dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.

11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;

mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.

12Ndayima pa malo wopanda zovuta

ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 26:1-12

En uskyldigs ydmyge bøn

1En sang af David.

Frikend mig, Herre, for jeg er uskyldig.

Jeg har altid sat min lid til dig.

2Se efter, hvad der bor i mit hjerte,

undersøg mine tanker og motiver.

3Jeg kender din trofaste nåde,

jeg ønsker at gøre din vilje.

4Jeg færdes ikke blandt de falske,

gør ikke de gudløse selskab.

5Jeg tager afstand fra de ondes planer,

jeg vil ikke have noget med dem at gøre.

6Jeg ønsker at bevare min uskyld,

så jeg kan nærme mig dit hellige alter.

7Der vil jeg synge dig en takkesang,

fortælle om alle dine undere.

8Herre, jeg elsker at komme til dit hus,

for det er der, jeg kan se din herlighed.

9Lad mig ikke dele skæbne med syndere,

døm mig ikke, som du dømmer voldsmænd,

10for de er altid ude på rov

og tager gerne imod bestikkelse.

11Men jeg lever oprigtigt og retskaffent.

Fri mig fra det onde og vær mig nådig.

12Mine fødder står på sikker grund,

og i folkets forsamling vil jeg prise dig, Herre.