Masalimo 26 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 26:1-12

Salimo 26

Salimo la Davide.

1Weruzeni Inu Yehova

pakuti ndakhala moyo wosalakwa.

Ndadalira Yehova

popanda kugwedezeka.

2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,

santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;

3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,

ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.

4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,

kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.

5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa

ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.

6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga

ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,

7kulengeza mofuwula za matamando anu

ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.

8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,

malo amene ulemerero wanu umapezekako.

9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,

moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,

10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,

dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.

11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;

mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.

12Ndayima pa malo wopanda zovuta

ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.

La Bible du Semeur

Psaumes 26:1-12

Fais-moi justice

1De David.

Fais-moi justice, ô Eternel, ╵car la vie que je mène ╵est sans reproche.

Je me confie en l’Eternel, ╵je ne faiblirai pas26.1 Autre traduction : sans faiblir..

2Sonde-moi, Eternel, ╵éprouve-moi

et examine ╵mon cœur et mes pensées.

3Je garde ton amour ╵présent à mon esprit,

et je conduis ma vie ╵selon ta vérité.

4Je ne vais pas m’asseoir ╵avec les hommes fourbes.

Je ne fréquente pas ╵les hypocrites.

5Je hais la compagnie ╵de ceux qui font le mal,

je ne vais pas m’asseoir ╵chez les méchants.

6Je laverai mes mains ╵en signe d’innocence26.6 Se laver les mains en public était un geste symbolique signifiant que l’on se déchargeait de toute responsabilité lorsqu’un crime avait été commis (Dt 21.7 ; Mt 27.24).

avant de m’approcher ╵de ton autel, ô Eternel,

7pour t’exprimer ╵ma gratitude,

et raconter ╵tes œuvres merveilleuses.

8O Eternel, ╵j’aime le lieu ╵où tu habites

et où ta gloire26.8 La gloire de Dieu dans le tabernacle (Ex 40.35) et plus tard dans le Temple (1 R 8.11) signalait la présence de l’Eternel lui-même (voir Ex 24.16 ; 32.22 ; cf. Jn 1.14). ╵a sa demeure !

9Ne lie donc pas mon sort ╵à celui des pécheurs,

ne m’ôte pas la vie ╵avec les assassins !

10Ils ont commis ╵des actes criminels,

ils se sont laissé acheter26.10 Autre traduction : elles cherchent à soudoyer..

11Mais moi je veux mener ╵une vie sans reproche.

Délivre-moi ╵et fais-moi grâce !

12Je marche sur le droit chemin26.12 Autre traduction : je me tiens sur un terrain ferme..

Oui, je veux te bénir, ╵ô Eternel, ╵au sein de l’assemblée.