Masalimo 25 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 25:1-22

Salimo 25

Salimo la Davide.

1Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.

2Ndimadalira Inu Mulungu wanga.

Musalole kuti ndichite manyazi

kapena kuti adani anga andipambane.

3Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye

sadzachititsidwa manyazi

koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi

ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.

4Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova,

phunzitseni mayendedwe anu;

5tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa,

pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga,

ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.

6Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu,

pakuti ndi zakalekale.

7Musakumbukire machimo a ubwana wanga

ndi makhalidwe anga owukira;

molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine,

pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.

8Yehova ndi wabwino ndi wolungama;

choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.

9Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama

ndipo amawaphunzitsa njira zake.

10Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika

kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.

11Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova,

khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.

12Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova?

Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.

13Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse,

ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.

14Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa;

amawulula pangano lake kwa iwowo.

15Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse,

pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.

16Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima,

pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.

17Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira;

masuleni ku zowawa zanga.

18Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga

ndipo mufafanize machimo anga onse.

19Onani mmene adani anga achulukira

ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.

20Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa;

musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndimathawira kwa Inu.

21Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze,

chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.

22Wombolani Israeli Inu Mulungu,

ku mavuto ake onse!

Korean Living Bible

시편 25:1-22

인도와 보호를 위한 기도

(다윗의 시)

1여호와여,

내가 주께 기도합니다.

2나의 하나님이시여,

내가 주를 의지합니다.

내가 부끄러움을

당하지 않게 하시고

내 원수들이 나를 이겨

기뻐하지 못하게 하소서.

3주를 신뢰하는 자는

부끄러움을 당하지 않으나

25:3 또는 ‘무고히 속이는 자는’주를 배반하는 자는

부끄러움을 당할 것입니다.

4여호와여,

주의 뜻을 나에게 보이시고

주의 길을 나에게 가르치소서.

5주의 진리로 나를

인도하시고 가르치소서.

주는 내 구원의 하나님이시므로

내가 하루 종일

주만 바라봅니다.

6여호와여, 옛날부터 보여 주신

주의 크신 자비와

사랑을 기억하소서.

7내 어릴 때의 죄와 허물을

기억하지 마시고

주의 한결같은 사랑과

선하심을 따라 나를 기억하소서.

8여호와는 선하시고 정직하시므로

죄인들에게 바른 길을 가르치시고

9겸손한 자들을

옳은 길로 인도하시며

그들에게 자기 뜻을 가르치신다.

10여호와께서는

그의 약속과 25:10 또는 ‘증거를’명령을 지키는

모든 사람들을

성실과 사랑으로 인도하시는구나.

11여호와여, 내 죄가 많을지라도

주의 이름을 위해 용서하소서.

12여호와를 두려운 마음으로

섬기는 자가 누구냐?

그가 택할 길을

하나님이 가르치시리라.

13그는 언제나 번영을 누리며 살고

그의 자손들은 땅을 상속하리라.

14여호와께서는 자기를

두려운 마음으로 섬기는 자들에게

친밀감을 가지시고

그 약속의 비밀을

그들에게 보이실 것이다.

15내가 항상 여호와를 바라보는 것은

그분만이 나를 위험에서

건져 줄 수 있기 때문이다.

16여호와여, 내가 외롭게

고통을 당하고 있습니다.

나에게 돌이키셔서

주의 자비를 베푸소서.

17내 마음의 고통이

점점 더해 갑니다.

나를 이 모든 괴로움에서

건져 주소서.

18나의 슬픔과 고통을 보시고

내 모든 죄를 용서하소서.

19수많은 나의 원수들을 보소서.

저들이 나를

몹시 미워하고 있습니다.

20나의 생명을 지키시고

나를 구하소서.

내가 주를 신뢰합니다.

내가 수치를 당하지 않게 하소서.

21내가 주를 바라봅니다.

주의 성실함과 정직함으로

나를 보호하소서.

22하나님이시여,

주의 백성 이스라엘을

그 모든 환난에서 구해 주소서.