Salimo 22
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.
1Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?
Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?
Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,
usikunso, ndipo sindikhala chete.
3Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;
ndinu matamando a Israeli.
4Pa inu makolo athu anadalira;
iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.
Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,
wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7Onse amene amandiona amandiseka;
amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8“Iyeyu amadalira Yehova,
musiyeni Yehovayo amulanditse.
Musiyeni Yehova amupulumutse
popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.
Munachititsa kuti ndizikudalirani
ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;
kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11Musakhale kutali ndi ine,
pakuti mavuto ali pafupi
ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12Ngʼombe zazimuna zandizungulira;
ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13Mikango yobangula pokadzula nyama,
yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14Ine ndatayika pansi ngati madzi
ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.
Mtima wanga wasanduka phula;
wasungunuka mʼkati mwanga.
15Mphamvu zanga zauma ngati phale,
ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;
mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16Agalu andizungulira;
gulu la anthu oyipa landizinga.
Alasa manja ndi mapazi anga.
17Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;
anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18Iwo agawana zovala zanga pakati pawo
ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19Koma Inu Yehova, musakhale kutali;
Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,
moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;
pulumutseni ku nyanga za njati.
22Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;
ndidzakutamandani mu msonkhano.
23Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!
Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!
Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza
kuvutika kwa wosautsidwayo;
Iye sanabise nkhope yake kwa iye.
Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.
Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26Osauka adzadya ndipo adzakhuta;
iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.
Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27Malekezero onse a dziko lapansi
adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,
ndipo mabanja a mitundu ya anthu
adzawerama pamaso pake,
28pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova
ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;
onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;
iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;
mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31Iwo adzalengeza za chilungamo chake
kwa anthu amene pano sanabadwe
pakuti Iye wachita zimenezi.
Dwom 22
Dawid dwom.
1Me Nyankopɔn, me Nyankopɔn, adɛn nti na woagyaw me?
Adɛn nti na me nkwagye ne wo ntam aware,
adɛn na mʼapinisi nsɛm ne wo ntam aware?
2Me Nyankopɔn, misu frɛ wo awia, nanso wunnye me so,
mefrɛ wo anadwo, nanso minnya ɔhome.
3Nanso wɔasi wo hene sɛ Ɔkronkronni;
wo na Israel kamfo wo.
4Wo mu na yɛn agyanom de wɔn werɛ hyɛe;
wogyee wo dii, na wugyee wɔn.
5Wosu frɛɛ wo na wugyee wɔn,
wɔde wɔn ho too wo so na woanni wɔn nhuammɔ.
6Nanso meyɛ osunson, na menyɛ onipa
nnipa bɔ me ahohora na wobu me animtiaa.
7Obiara a ohu me di me ho fɛw;
wotwa me adapaa, wosow wɔn ti ka se:
8“Ɔde ne ho to Awurade so;
ma Awurade mmegye no.
Ma ɔmmɛboa no,
efisɛ ɔwɔ no mu anigye.”
9Wo na wuyii me fii awotwaa mu bae
na womaa me de me ho too wo so
bere a mitua me na nufu ano mpo.
10Efi mʼawo mu na wɔde me too wo so;
efi me na yafunu mu, woayɛ me Nyankopɔn.
11Ntwe wo ho mfi me ho!
Efisɛ amane abɛn
na ɔboafo nni baabi.
12Anantwinini bebree atwa me ho ahyia;
Basan anantwinini a wɔn ho yɛ den atwa me ho ahyia.
13Gyata a wɔbobɔ mu na wɔtetew wɔn hanam mu
abuebue wɔn anom tɛtrɛɛ de kyerɛ me.
14Wɔahwie me agu sɛ nsu,
na me nnompe nyinaa ahodwow.
Me koma adan amane;
anan wɔ me mu.
15Mʼanom ayow te sɛ kyɛmfɛre mu.
Na me tɛkrɛma atare mʼanom.
Wode me to owu mfutuma mu.
16Akraman atwa me ho ahyia,
nnebɔneyɛfo kuw atwa me ahyia,
wɔahwirew me nsa ne mʼanan mu.
17Me nnompe nyinaa gu petee mu;
Mʼatamfo hwɛ me haa na wɔserew me.
18Wɔkyɛ me atade mu fa,
na wɔbɔ me ntama so ntonto.
19Na wo, Awurade, ntwe wo ho;
wone mʼahoɔden, bra ntɛm bɛboa me.
20Gye me kra fi afoa ano;
gye me nkwa a ɛsom bo no fi akraman tumi ase.
21Gye me nkwa fi gyata anom;
gye me fi ɛko mmɛn so.
22Mɛbɔ wo din akyerɛ me nuanom;
mɛkamfo wo wɔ wɔn a wɔahyia hɔ no nyinaa anim.
23Monkamfo Awurade, mo a musuro no no!
Mo a moyɛ Yakob asefo, monhyɛ no anuonyam!
Mo Israel asefo nyinaa, munni no ni!
24Ommuu nʼani nguu
ɔmanehunufo ateetee so ɛ,
ɔmfaa nʼanim nhintaw no;
na mmom watie ne sufrɛ a ɔde rehwehwɛ mmoa no.
25Me botae a mede yi wo ayɛ wɔ bagua mu no fi wo;
medi me bɔhyɛ so wɔ wɔn a wosuro wo no anim.
26Ahiafo bedidi na wɔamee;
wɔn a wɔhwehwɛ Awurade beyi no ayɛ,
mo koma nnya nkwa daa.
27Asase ano nyinaa
bɛkae akɔ Awurade nkyɛn,
na amanaman no mmusua nyinaa
bɛkotow nʼanim,
28efisɛ tumi wɔ Awurade
na odi amanaman so hene.
29Asase so adefo nyinaa bedidi na wɔasɔre no;
wɔn a wɔkɔ dɔte mu nyinaa bebu nkotodwe nʼanim,
wɔn a wɔrentumi mma nkwa mu.
30Nkyirimma nyinaa bɛsom no;
wɔbɛka Awurade ho asɛm akyerɛ awo ntoatoaso a edidi so.
31Wɔbɛka ne trenee akyerɛ
nnipa a wonnya nwoo wɔn
efisɛ ɔno na wayɛ.